Yobu
2 Anthu onyoza andizungulira,+
Ndipo diso langa likuyenera kuyangʼanitsitsa* khalidwe lawo lopanduka.
3 Chonde, landilani chikole changa ndipo muchisunge.
Kodi pali winanso amene angagwirane nane chanza nʼkulonjeza kuti andithandiza?+
5 Anthu amenewa amauza anzawo kuti agawana nawo chuma chawo,
Pamene ana awo akulephera kuona bwinobwino chifukwa cha njala.
7 Chifukwa cha kuzunzika, maso anga ayamba kuchita mdima.+
Manja ndi miyendo yanga zakhala ngati mthunzi.
8 Anthu owongoka mtima akuyangʼana zimenezi modabwa,
Ndipo munthu wosalakwa wakhumudwa chifukwa cha anthu oipa.*
9 Wolungama akuyendabe panjira yake,+
Ndipo amene ali ndi manja oyera, mphamvu zake zikuwonjezereka.+
10 Komabe, nonsenu mungathe kubwera nʼkuyambiranso kundinena,
Chifukwa sindikuonapo aliyense wanzeru pakati panu.+
12 Anzanga akumasintha usiku kuti ukhale masana.
Iwo akunena kuti, ‘Chifukwa choti kuli mdima, kuwala kuyenera kuti kwayandikira.’
14 Ndidzaitana dzenje*+ kuti, ‘Ndinu bambo anga!’
Kwa mphutsi ndidzati, ‘Mayi anga ndi mlongo wanga!’
15 Ndiye chiyembekezo changa chili kuti?+
Kodi pali amene akuona kuti ndili ndi chiyembekezo?