Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 24
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Ukwati komanso kutha kwa ukwati (1-5)

      • Kulemekeza moyo (6-9)

      • Kuganizira osauka (10-18)

      • Malamulo okhudza kukunkha (19-22)

Deuteronomo 24:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 5:31, 32; Mko 10:4, 11
  • +Mki 2:16; Mt 1:19; 19:3-8

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    “Wotsatira Wanga,” ptsa. 104-105

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    12/2018, tsa. 11

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    8/2016, ptsa. 10-11

    Yesu—Ndi Njira, tsa. 222

    Nsanja ya Olonda,

    9/1/2008, tsa. 25

    8/15/1993, ptsa. 4-5

Deuteronomo 24:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 21:7

Deuteronomo 24:3

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “sakumufunanso.”

Deuteronomo 24:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 20:7; Miy 5:18; Mla 9:9

Deuteronomo 24:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:26, 27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/1/2014, tsa. 7

    9/15/2004, tsa. 26

Deuteronomo 24:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 37:28; 40:15
  • +Eks 21:16
  • +De 19:18, 19; 21:20, 21

Deuteronomo 24:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Mawu a Chiheberi amene anawamasulira kuti “khate” amatanthauza zambiri kuphatikizapo matenda apakhungu osiyanasiyana opatsirana. Angaphatikizenso matenda ena opezeka mʼzovala ndi mʼnyumba.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 13:2, 15; Mko 1:44; Lu 17:14

Deuteronomo 24:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 12:10, 15

Deuteronomo 24:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 15:7, 8; Miy 3:27

Deuteronomo 24:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yob 24:9, 10

Deuteronomo 24:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:26, 27

Deuteronomo 24:14

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmageti anu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 25:39, 43; Miy 14:31

Deuteronomo 24:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:13; Yer 22:13; Mt 20:8
  • +Miy 22:22, 23; Yak 5:4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    1/2018, tsa. 32

Deuteronomo 24:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Mb 25:3, 4
  • +Eze 18:20

Deuteronomo 24:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:21, 22
  • +Eks 22:26, 27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    2/2019, tsa. 24

Deuteronomo 24:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 5:15

Deuteronomo 24:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:9; 23:22; Ru 2:16; Sl 41:1
  • +De 15:7, 10; Miy 11:24; 19:17; Lu 6:38; 2Ak 9:6; 1Yo 3:17

Deuteronomo 24:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:10; De 26:13

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 24:1Mt 5:31, 32; Mko 10:4, 11
Deut. 24:1Mki 2:16; Mt 1:19; 19:3-8
Deut. 24:2Le 21:7
Deut. 24:5De 20:7; Miy 5:18; Mla 9:9
Deut. 24:6Eks 22:26, 27
Deut. 24:7Ge 37:28; 40:15
Deut. 24:7Eks 21:16
Deut. 24:7De 19:18, 19; 21:20, 21
Deut. 24:8Le 13:2, 15; Mko 1:44; Lu 17:14
Deut. 24:9Nu 12:10, 15
Deut. 24:10De 15:7, 8; Miy 3:27
Deut. 24:12Yob 24:9, 10
Deut. 24:13Eks 22:26, 27
Deut. 24:14Le 25:39, 43; Miy 14:31
Deut. 24:15Le 19:13; Yer 22:13; Mt 20:8
Deut. 24:15Miy 22:22, 23; Yak 5:4
Deut. 24:162Mb 25:3, 4
Deut. 24:16Eze 18:20
Deut. 24:17Eks 22:21, 22
Deut. 24:17Eks 22:26, 27
Deut. 24:18De 5:15
Deut. 24:19Le 19:9; 23:22; Ru 2:16; Sl 41:1
Deut. 24:19De 15:7, 10; Miy 11:24; 19:17; Lu 6:38; 2Ak 9:6; 1Yo 3:17
Deut. 24:20Le 19:10; De 26:13
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 24:1-22

Deuteronomo

24 “Ngati mwamuna wakwatira mkazi koma mkaziyo sakumusangalatsa chifukwa wamupeza ndi vuto linalake, azimulembera kalata yothetsera ukwati+ nʼkumupatsa, ndipo azimuchotsa panyumba pake.+ 2 Akachoka panyumba ya mwamunayo, angathe kupita kukakhala mkazi wa mwamuna wina.+ 3 Ngati mwamuna wachiwiriyo wadana naye* mkaziyo ndipo wamulembera kalata yothetsera ukwati nʼkumupatsa kenako nʼkumuthamangitsa panyumba pake, kapena ngati mwamuna wachiwiriyo, amene anakwatira mkaziyo wamwalira, 4 mwamuna woyamba amene anamuthamangitsa uja sadzaloledwa kumutenganso kuti akhale mkazi wake pambuyo poti waipitsidwa, chifukwa zimenezo ndi zonyansa kwa Yehova. Musamachite machimo amenewa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti likhale cholowa.

5 Mwamuna akakwatira kumene, asamakhale mʼgulu lankhondo, ndiponso asamapatsidwe ntchito iliyonse. Azikhala kunyumba kwa chaka chimodzi osachita zinthu zimenezi kuti asangalatse mkazi wake.+

6 Munthu asamalande mnzake mphero kapena mwala waungʼono woperera ngati chikole cha ngongole,+ chifukwa kutenga zinthu zimenezi kuli ngati kutenga moyo wa munthu ngati chikole.

7 Munthu akapezeka ataba mmodzi mwa abale ake, Aisiraeli, ndipo wamuchitira nkhanza nʼkumugulitsa,+ wakuba munthuyo ayenera kufa.+ Muzichotsa woipayo pakati panu.+

8 Ngati kwabuka matenda a khate,* muzionetsetsa kuti mukuchita zinthu zonse mogwirizana ndi zimene Alevi omwe ndi ansembe akulangizani.+ Muzionetsetsa kuti mukuchita mogwirizana ndi zimene ndinawalamula. 9 Muzikumbukira zimene Yehova Mulungu wanu anachitira Miriamu panjira mutatuluka mʼdziko la Iguputo.+

10 Ngati mwapereka ngongole ya mtundu uliwonse kwa mnzanu,+ musamalowe mʼnyumba yake kukatenga chimene wanena kuti akupatsani kuti chikhale chikole. 11 Muziima panja, ndipo munthu amene munamupatsa ngongoleyo azikubweretserani yekha chikolecho panjapo. 12 Ndipo ngati munthuyo ndi wosauka, musamagone ndi chinthu chake chimene wakupatsani kuti chikhale chikolecho.+ 13 Muzionetsetsa kuti mwamubwezera chikolecho dzuwa likangolowa, kuti azipita kukagona ali ndi chofunda chake.+ Mukatero iye adzakudalitsani, ndipo mudzakhala mutachita chilungamo pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

14 Musamabere mwachinyengo waganyu yemwe ndi wovutika ndiponso wosauka, kaya akhale mmodzi wa abale anu kapena mlendo amene akukhala mʼdziko lanu, amene ali mʼmizinda yanu.*+ 15 Muzimupatsa malipiro ake tsiku lomwelo dzuwa lisanalowe,+ chifukwa iye ndi wosauka ndipo akudalira malipiro ake omwewo kuti akhale ndi moyo. Mukapanda kutero adzafuula kwa Yehova chifukwa cha zimene inuyo mwamuchitira ndipo mudzapezeka kuti mwachimwa.+

16 Abambo asamaphedwe chifukwa cha zimene ana awo achita, ndipo ana asamaphedwe chifukwa cha zimene abambo awo achita.+ Munthu aliyense aziphedwa chifukwa cha tchimo lake.+

17 Musamapotoze chiweruzo cha mlandu wa mlendo kapena mlandu wa mwana wamasiye,+ ndipo musamalande chovala cha mkazi wamasiye kuti chikhale chikole.+ 18 Muzikumbukira kuti munali akapolo mʼdziko la Iguputo, ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko.+ Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.

19 Mukaiwala mtolo wa tirigu pokolola mʼmunda mwanu, musamabwerere kukatenga mtolowo. Muzisiyira mlendo wokhala mʼdziko lanu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye.+ Muzichita zimenezi kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa chilichonse chimene mukuchita.+

20 Mukamakwapula mitengo ya maolivi pokolola, musamabwereze kukwapula nthambi zimene mwakwapula kale. Zimene zatsala zizikhala za mlendo wokhala mʼdziko lanu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye.+

21 Mukamakolola mphesa mʼmunda wanu, musamabwerere kukakunkha zotsala. Mphesa zotsalazo zizikhala za mlendo wokhala mʼdziko lanu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye. 22 Muzikumbukira kuti munali akapolo mʼdziko la Iguputo. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena