Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 1
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI MUMSASA WA MFUMU SOLOMO (1:1–3:5)

        • Nyimbo yoposa nyimbo zonse (1)

        • Mtsikana (2-7)

        • Ana aakazi a ku Yerusalemu (8)

        • Mfumu (9-11)

          • “Ife tikupangira zokongoletsa zagolide” (11)

        • Mtsikana (12-14)

          • ‘Wachikondi wanga ali ngati kathumba konunkhira ka mule’ (13)

        • Mʼbusa (15)

          • “Ndiwe wokongola wokondedwa wanga”

        • Mtsikana (16, 17)

          • “Iwenso ndiwe wooneka bwino, wachikondi wanga” (16)

Nyimbo ya Solomo 1:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 4:29, 32

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 17

Nyimbo ya Solomo 1:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, ptsa. 30-31

    11/15/2006, tsa. 18

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 1:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 27:9; Mla 9:8; Nym 5:5
  • +Mla 7:1

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, ptsa. 30-31

    11/15/2006, tsa. 18

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 1:4

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “Tiye tikambirane za.”

Nyimbo ya Solomo 1:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 120:5; Eze 27:21
  • +Eks 36:14

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 18

Nyimbo ya Solomo 1:6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 32

    Galamukani!,

    4/8/1994, ptsa. 24-25

Nyimbo ya Solomo 1:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “nsalu yovala kumutu polira maliro.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 6:3

Nyimbo ya Solomo 1:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 10:28; 2Mb 1:16, 17; Nym 6:4

Nyimbo ya Solomo 1:10

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “Masaya ako ndi okongola ndi nkhata zatsitsi.”

Nyimbo ya Solomo 1:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “zovala kumutu.”

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 1:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “Nado wanga.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:13, 14

Nyimbo ya Solomo 1:13

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 30:23, 25; Est 2:12; Sl 45:8; Nym 4:6; 5:13

Nyimbo ya Solomo 1:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:13
  • +Yos 15:20, 62; 1Sa 23:29; 2Mb 20:2

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/1/1989, tsa. 17

Nyimbo ya Solomo 1:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:1; 5:2

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 18

Nyimbo ya Solomo 1:16

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “ndiwe wokongola.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 5:10

Nyimbo ya Solomo 1:17

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “Nyumba yathu yabwino kwambiri.”

  • *

    Mtengo wa junipa ndi wofanana ndi mtengo wa mkungudza.

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 1:11Mf 4:29, 32
Nyimbo 1:2Nym 4:10
Nyimbo 1:3Miy 27:9; Mla 9:8; Nym 5:5
Nyimbo 1:3Mla 7:1
Nyimbo 1:5Sl 120:5; Eze 27:21
Nyimbo 1:5Eks 36:14
Nyimbo 1:7Nym 6:3
Nyimbo 1:91Mf 10:28; 2Mb 1:16, 17; Nym 6:4
Nyimbo 1:12Nym 4:13, 14
Nyimbo 1:13Eks 30:23, 25; Est 2:12; Sl 45:8; Nym 4:6; 5:13
Nyimbo 1:14Nym 4:13
Nyimbo 1:14Yos 15:20, 62; 1Sa 23:29; 2Mb 20:2
Nyimbo 1:15Nym 4:1; 5:2
Nyimbo 1:16Nym 5:10
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 1:1-17

Nyimbo ya Solomo

1 Nyimbo yoposa nyimbo zonse, nyimbo ya Solomo:+

 2 “Undikise ndi milomo yako,

Chifukwa chikondi chimene umandisonyeza chimaposa vinyo.+

 3 Kununkhira kwa mafuta ako ndi kosangalatsa.+

Dzina lako lili ngati mafuta onunkhira amene athiridwa pamutu.+

Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda.

 4 Nditenge, tiye tithawe.

Chifukwatu mfumu yandipititsa mʼzipinda zake zamkati.

Tiye tikondwere komanso kusangalalira limodzi.

Tiye titamande* chikondi chimene umandisonyeza kuposa kutamanda vinyo.

Mpake kuti atsikana amakukonda.

 5 Inu ana aakazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda koma wokongola,

Ngati matenti a ku Kedara+ komanso nsalu za matenti+ a Solomo.

 6 Musandiyangʼanitsitse chifukwa chakuti ndada,

Ndi dzuwatu landidetsali.

Ana aamuna a mayi anga anandikwiyira.

Choncho anandiika kuti ndiziyangʼanira minda ya mpesa

Moti sindinathe kusamalira munda wanga wa mpesa.

 7 Tandiuze, iwe amene ndimakukonda kwambiri,

Ndiuze kumene umakadyetsera ziweto zako,+

Kumene umakagonetsa ziweto masana.

Kodi ndikhalirenji ngati mkazi amene wafunda nsalu kumutu*

Pakati pa magulu a ziweto za anzako?”

 8 “Ngati iweyo sukudziwa, iwe mkazi wokongola kwambiri kuposa akazi onse,

Tsatira mapazi a ziweto

Ndipo ukadyetse mbuzi zako zingʼonozingʼono pafupi ndi matenti a abusa.”

 9 “Iwe wokondedwa wanga, kwa ine uli ngati hatchi yaikazi yapamagaleta a Farao.+

10 Masaya ako amaoneka bwino ukavala zodzikongoletsera,*

Ndipo khosi lako limaoneka bwino ukavala mikanda.

11 Ife tikupangira zokongoletsa* zagolide

Zokhala ndi mikanda yasiliva.”

12 “Pamene mfumu yakhala patebulo lake lozungulira,

Mafuta anga onunkhira*+ akutulutsa kafungo kosangalatsa.

13 Wachikondi wanga ali ngati kathumba konunkhira ka mule* kwa ine.+

Iye amakhala pakati pa mabere anga usiku wonse.

14 Kwa ine, wachikondi wanga ali ngati maluwa a hena+

Mʼminda ya mpesa ya ku Eni-gedi.”+

15 “Ndiwe wokongola wokondedwa wanga.

Ndiwe chiphadzuwa. Maso ako ali ngati maso a njiwa.”+

16 “Iwenso ndiwe wooneka bwino,* wachikondi wanga komanso ndiwe wosangalatsa.+

Bedi lathu ndi lamasamba ofewa.

17 Nyumba yathu* inamangidwa ndi mitengo ya mkungudza,

Ndipo kudenga kwake kuli mitengo ya junipa.”*

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena