Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 1/11 tsamba 22-31
  • Zoti Banja Likambirane

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zoti Banja Likambirane
  • Galamukani!—2011
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Chithunzichi Chalakwika Pati?
  • Sungani Kuti Muzikumbukira
  • Anthu ndi Mayiko
  • Zithunzi Zoti Ana Apeze
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2012
  • Zimene Yoswa Anakumbukira
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Iye Amafuna Kuti Zinthu Zizitiyendera Bwino
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2012
Onani Zambiri
Galamukani!—2011
g 1/11 tsamba 22-31

Zoti Banja Likambirane

Kodi Chithunzichi Chalakwika Pati?

Werengani Yohane 6:5-13. Tchulani zinthu zitatu zomwe zalakwika pachithunzichi. Lembani mayankho anu m’munsimu. Ndipo malizitsani kujambula chithunzichi pochichekenira.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

3. ․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi Yesu anauza ophunzira ake kuti asonkhanitse chiyani, ndipo n’chifukwa chiyani? Kodi zimenezi zikukuphunzitsani chiyani zokhudza Yesu? Kodi mungatani kuti musamawononge zakudya kapena zinthu zina?

ZOTI BANJA LICHITIRE PAMODZI:

Werengani nkhaniyo pamodzi m’Baibulo. Ngati n’kotheka, sankhani munthu mmodzi kuti akhale munthu wofotokoza nkhaniyo, wina akhale Yesu, wina Filipi ndipo wina akhale Andireya.

Sungani Kuti Muzikumbukira

Dulani, pindani pakati n’kusunga

KHADI LA BAIBULO 1 YOSWA

MAFUNSO

A. Kodi Yoswa ndi asilikali ake anatani kuti athe kugwetsa makoma a Yeriko?

B. Malizitsani mawu a Yoswa awa: “Ine ndi a m’nyumba yanga . . . ”

C. Kodi Yoswa ankadziwikanso ndi mayina ena ati?

[Tchati]

4026 B.C.E. 1 C.E. 98 C.E.

Kulengedwa kwa Adamu Anakhala ndi moyo Baibulo linamalizidwa

cha m’ma 1500’s B.C.E. kulemba

[Mapu]

Anachoka ku Iguputo kupita ku Dziko Lolonjezedwa

IGUPUTO

DZIKO LOLONJEZEDWA

YOSWA

ANALI NDANI?

Mwana wa Nuni. Anali mtumiki wa Mose, kenako anasankhidwa kuti atsogolere mtundu wa Isiraeli. (Ekisodo 33:11; Deuteronomo 34:9; Yoswa 1:1, 2) Yoswa anatsogolera anthu a Mulungu molimba mtima popita ku Dziko Lolonjezedwa. Ankakhulupirira malonjezo a Yehova, ankamvera malangizo ake, ndipo ankamutumikira mokhulupirika.

MAYANKHO

A. Anamvera Mulungu poguba kuzungulira mzindawo.—Yoswa 6:1-27.

B. “. . . tizitumikira Yehova.”—Yoswa 24:15.

C. Hoshiya ndi Yehoswa.—Numeri 13:8, 16.

Anthu ndi Mayiko

4. Dzina langa ndi Victor. Ndili ndi zaka 7 ndipo ndimakhala ku Malawi. Dzikoli limapezeka ku Africa. Kodi mukudziwa kuti ku Malawi kuli Mboni za Yehova zingati? Kodi ziliko pafupifupi 750, 7,500, kapena 75,000?

5. Kodi ndi kadontho kati kamene kakusonyeza dziko limene ndimakhala? Jambulani mzere wozungulira kadonthoko, ndipo kenako jambulani kadontho kosonyeza kumene inuyo mumakhala kuti muone kuyandikana kwa dziko lanu ndi la Malawi.

A

B

C

D

Zithunzi Zoti Ana Apeze

Pezani zithunzi izi m’magazini ino. Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

● Mayankho a mafunso a patsamba 30 ndi 31 ali patsamba 22.

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 30 ndi 31

1. Wagwira mbale ya zakudyayo ayenera kukhala mnyamata, osati mtsikana.

2. M’mbalemo muyenera kukhala buledi musanu, osati maapozi asanu.

3. Muyenera kukhala nsomba ziwiri, osati chimanga chiwiri.

4. 75,000.

5. C.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena