Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w94 5/1 tsamba 32
  • Tikulandirani ku Msonkhano Wachigawo wa “Mantha Aumulungu”!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tikulandirani ku Msonkhano Wachigawo wa “Mantha Aumulungu”!
  • Nsanja ya Olonda—1994
  • Nkhani Yofanana
  • Msonkhano Wachigawo wa 1995 wa “Atamandi Achimwemwe”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Fikani pa Msonkhano Wachigawo Wakuti “Mantha Aumulungu”!
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Msonkhano Wachigawo Wakuti “Mantha Aumulungu” wa 1994
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
  • Zokumbutsa za Msonkhano Wachigawo wa 1998 Wakuti: “Njira ya Moyo ya Mulungu.”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1994
w94 5/1 tsamba 32

Tikulandirani ku Msonkhano Wachigawo wa “Mantha Aumulungu”!

INDE, nthaŵi ya misonkhano yachigawo ya 1994 ya Mboni za Yehova ikuyandikira. Kuyambira June 1994 mpaka January 1995, programu ya msonkhano ya masiku atatu idzachitidwa m’mizinda mazana ambiri pa dziko lonse​—kuyambira ku North America, kenako ku Eastern ndi Western Europe, Asia, Central ndi South America, Afirika, Australia, ndi zisumbu za m’nyanja.

Ndi mutu wotokosa maganizo chotani nanga​—“Mantha Aumulungu”! Ameneŵa sali mantha oipa a munthu amene moyo wake uli pangozi koma kuwopa Mulungu, mantha amene amapereka mtendere wa maganizo ndi chisangalalo. Mwambi wa Baibulo umati: “Mphotho ya chifatso ndi kuopa Yehova, ndiy[o] chuma, ndi ulemu, ndi moyo.” (Miyambo 22:4) Kodi kuopa Mulungu kungabweretse motani “chuma, ndi ulemu, ndi moyo”? Zimenezo zidzaonekera bwino pamene mutu wa msonkhanowo udzafutukulidwa m’masiku atatu odzaza ndi nkhani, makambitsirano, zitsanzo, ndi drama.

Mtumwi Paulo analemba kuti sitiyenera ‘kuleka kusonkhana kwathu pamodzi.’ (Ahebri 10:25) Mboni za Yehova zimaona zimenezo mwamphamvu, zikumasonkhana nthaŵi zitatu pa mlungu kaamba ka phunziro la mpingo ndi kulambira. Komabe, msonkhano wachigawo wa pachaka uli wapadera. Izo zimauyembekezera mwachidwi ndi kulankhula za uwo kwa miyezi yambiri pambuyo pake. Tikuitanani mwaubwenzi, mosasamala kanthu za chipembedzo chanu, kudzagwirizana nawo pa msonkhano wawo ndi kusangalala ndi ubwenzi weniweni Wachikristu ndi chidziŵitso chofunika chauzimu. Chiŵalo cha mpingo wa Mboni za Yehova wa kwanuko chidzakhala chosangalala kukuuzani malo ndi nthaŵi imene msonkhano wakufupi nanu udzachitidwa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena