Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp16 No. 3 tsamba 16
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mulungu ali ndi dzina?
  • Kodi kutchula dzina la Mulungu n’kulakwa?
  • Dzina la Mulungu
    Galamukani!—2017
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kugwiritsa Ntchito Dzina la Mulungu?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Chifukwa Chake Tiyenera Kudziwa Dzina la Mulungu
    Dzina la Mulungu Limene Lidzakhala Kosatha
  • Kodi Dzina la Mulungu Ndi Ndani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2019
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
wp16 No. 3 tsamba 16
Mmene dzina la Mulungu linkalembedwera m’mipukutu yakale ya Baibulo

Mmene dzina la Mulungu linkalembedwera m’mipukutu yakale ya Baibulo (mwawalitsidwamo)

Kodi Baibulo Limanena Zotani?

Kodi Mulungu ali ndi dzina?

ANTHU ENA AMAKHULUPIRIRA kuti Mulungu alibe dzina ndipo ena amanena kuti dzina lake ndi Mulungu kapena Ambuye. Pomwe enanso amanena kuti Mulungu ali ndi mayina ambirimbiri. Kodi inuyo mukuganiza bwanji?

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

“Inu, amene dzina lanu ndinu Yehova, Inu nokha ndinu Wam’mwambamwamba, wolamulira dziko lonse lapansi.”—Salimo 83:18.

MFUNDO ZINANSO ZOMWE BAIBULO LIMANENA

  • N’zoona kuti Mulungu ali ndi mayina audindo ambiri koma ali ndi dzina lenileni limodzi lomwe anadzipatsa.—Ekisodo 3:15.

  • Mulungu si wosamvetsetseka ndipo amafuna kuti timudziwe bwino.—Machitidwe 17:27.

  • Ngati munthu akufuna kukhala pa ubwenzi ndi Mulungu, choyamba amafunika kudziwa dzina lake.—Yakobo 4:8.

Kodi kutchula dzina la Mulungu n’kulakwa?

KODI MUNGAYANKHE BWANJI?

  • Inde

  • Ayi

  • Mwina

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

“Usagwiritse ntchito dzina la Yehova Mulungu wako mosasamala.” (Ekisodo 20:7) Choncho n’kulakwa kugwiritsa ntchito dzina la Mulungu mopanda ulemu.—Yeremiya 29:9.

MFUNDO ZINANSO ZOMWE BAIBULO LIMANENA

  • Yesu ankadziwa komanso kutchula dzina la Mulungu.—Yohane 17:25, 26.

  • Mulungu amafuna kuti tizitchula dzina lake.—Salimo 105:1.

  • Adani a Mulungu safuna kuti anthu azigwiritsa ntchito dzina la Mulungu.—Yeremiya 23:27.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 10 m’buku ili, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?, lofalitsidwa ndi a Mboni za Yehova

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena