Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w18 July tsamba 32
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Akulu, Weruzani Mwachilungamo
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Bokosi la Mafunso
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Akulu—Samalirani Gulu la Mulungu Mokoma Mtima!
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Kuyesetsa Kuti Anthu Mumpingo Apitirize Kukhala Amtendere Komanso Oyera
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
w18 July tsamba 32

Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Ngati mwamuna ndi mkazi amene sali pa banja atakhala limodzi usiku wonse popanda zifukwa zomveka, kodi tingati achita tchimo lofunika komiti yoweruza?

Panyumba inayake usiku pali magalimoto awiri

Inde. Ngati anthuwo akhala limodzi popanda zifukwa zomveka, komiti yoweruza mlandu ikhoza kupangidwa chifukwa umenewu ungakhale umboni wosonyeza kuti anthuwo achita dama.​—1 Akor. 6:18.

Bungwe la akulu liyenera kufufuza bwino nkhaniyo kuti lidziwe ngati pangafunike komiti yoweruza kapena ayi. Mwachitsanzo, kodi anthuwo akhala ali pa chibwenzi? Kodi m’mbuyomo anapatsidwapo malangizo pa nkhani ya mmene amachitira zinthu pa chibwenzi chawo? N’chifukwa chiyani anakhala limodzi usiku wonse? Kodi anachita kukonzeratu kuti akakhale limodzi usikuwo? Nanga panali njira ina imene akanatsatira kuti asakhale limodzi? Kapena panali vuto linalake ladzidzidzi limene linachititsa kuti asachitire mwina koma akhale limodzi usikuwo? (Mlal. 9:11) Kodi anagona bwanji? Popeza zochitika zimasiyana pa nkhani iliyonse, akulu ayenera kufufuza bwino n’kumaganizira zifukwa zonse zimene zinachititsa.

Pambuyo pofufuza zifukwa zonse, bungwe la akulu lingaone ngati pangafunike kupanga komiti yoweruza.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena