Mukamaona Kuti Simungathenso Kupirira
Mwachitsanzo, ku United States kutawomba mphepo yamkuntho, katundu wambiri wa Sallya anawonongeka. Iye anati: “Ndinasowa mtengo wogwira, moti ndinkaona kuti sindingathenso kupirira.”
Vuto lina lingakhale imfa ya munthu amene timam’konda. Janice yemwe amakhala ku Australia anati: “Ana anga aamuna awiri atamwalira, ndinamva ululu woopsa mumtima mwanga. Ndinapemphera kwa Mulungu kuti: ‘Chonde, sindithanso kupirira. Ndiloleni ndingofa chifukwa sindikufunanso kukhala ndi moyo.’”
Nayenso Daniel anasokonezeka maganizo atazindikira kuti mkazi wake wachita chigololo. Iye anati: “Mkazi wanga atavomera kuti anachitadi zimenezi, zinangokhala ngati ndabayidwa ndi mpeni mumtimamu. Kwa miyezi ingapo ndinkamvabe ululu umenewu.”
Nsanja ya Olonda ino ifotokoza zimene zingatithandize kupirira
Pakachitika ngozi zadzidzidzi
Munthu amene timamukonda akamwalira
Mwamuna kapena mkazi wathu akakhala wosakhulupirika
Ngati tikudwala kapena kudwazika matenda aakulu
Ngati tikuona kuti bola kungofa
Choyamba, tiyeni tione zimene zingatithandize pakachitika ngozi zadzidzidzi.
a Munkhanizi mayina ena asinthidwa.