Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 7/14 tsamba 4
  • Kodi Mungatani Mutakumana Ndi Vuto Lalikulu?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mungatani Mutakumana Ndi Vuto Lalikulu?
  • Galamukani!—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Mawu Oyamba
    Galamukani!—2020
  • Kodi N’chiyani Chingandithandize Ndikakumana ndi Mavuto?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Mukakumana ndi Mavuto Amwadzidzidzi
    Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 7/14 tsamba 4
1. Zinthu zotsalira pa nthawi ya tsoka lachilengedwe; 2. Bedi la kuchipatala; 3. Magalimoto agundana

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUNGATANI MUTAKUMANA NDI VUTO LALIKULU?

Kodi Mungatani Mutakumana Ndi Vuto Lalikulu?

ANTHUFE tikhoza kukumana ndi vuto lalikulu pa nthawi imene sitikuyembekezera. Ndipo zimenezi zikhoza kuchitikira aliyense, ngakhale munthu wolemera.

BAIBULO LIMANENA KUTI:

“Anthu othamanga kwambiri sapambana pampikisano, amphamvu sapambana pankhondo, anzeru sapeza chakudya, omvetsa zinthu nawonso sapeza chuma, ndipo ngakhale odziwa zinthu sakondedwa, chifukwa nthawi yatsoka ndi zinthu zosayembekezereka zimagwera onsewo.”—Mlaliki 9:11.

Popeza aliyense akhoza kukumana ndi vuto lalikulu, funso ndi lakuti: Kodi inuyo zimenezi zitakuchitikirani mungatani? Mwachitsanzo, kodi mungatani:

  • Katundu wanu yense atawonongeka pa ngozi zamwadzidzidzi monga kusefukira kwa madzi?

  • Atakupezani ndi matenda aakulu?

  • Munthu wa m’banja lanu atamwalira?

A Mboni za Yehova, omwe amafalitsa magaziniyi, amakhulupirira kuti Baibulo lingakuthandizeni kudziwa zoyenera kuchita zoterezi zikachitika. Baibulo lingakuthandizeninso kudziwa zimene mungachite kuti mukhale ndi chiyembekezo. (Aroma 15:4) Zitsanzo zotsatirazi zikusonyeza umboni wa zimenezi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena