Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/97 tsamba 2
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Nkhani Yofanana
  • Ndingatani Ngati Anzanga Akundikakamiza Kugonana?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Kodi Nchifukwa Ninji Kuli Kovuta Kwambiri Kuchotsa Maganizo Anga pa Osiyana Nawo Ziŵalo?
    Galamukani!—1994
  • Muzikambirana ndi Ana Anu Nkhani Zokhudza Kugonana
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Kodi Kugonana M’kamwa Kumakhaladi Kugonana?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
km 5/97 tsamba 2

Bokosi la Mafunso

◼ Ngati ndife mbale tili ndi mlongo mu utumiki wathu, kapenanso tapeza mkazi panyumba tili tokha; kayanso ndife mlongo tili ndi mbale, kapenanso tapeza mwamuna tili tokha, kodi tifunikira kusamala chiyani?

Tili ndi chifukwa chabwino chokhulupirira kuti abale ndi alongo athu amafuna kudzisunga kwambiri pamakhalidwe awo. Komabe, tikukhala m’dziko lonyansa, lololera zoipa lomwe ndi losadziletsa pamakhalidwe ake. Pamene kuli koti tili ndi zolinga zabwino, tiyenera kusamala nthaŵi zonse kuti tipeŵe chitonzo kapena kuchita kanthu kena kosayenera. Zimenezi zikuphatikizapo kusamala pamene tili mu utumiki.

Mu utumiki wakumunda kaŵirikaŵiri abale amapeza akazi kapena alongo kupeza amuna amene amasonyeza chooneka ngati chidwi chenicheni cha choonadi. Ngati pakhomopo tafikapo tokha ndipo mulibenso wina m’nyumbamo, kaŵirikaŵiri zimakhala bwino kwambiri kumlalikira muli pakhomo pompo m’malo moloŵa m’nyumba. Ngati wakondwa nazo, mungakonze kudzabwererako ndi wofalitsa wina kapena pamene ena a m’banjalo aliponso. Ngati zimenezo nzosatheka, kungakhale kwanzeru kumsiya mwini nyumbayo m’manja mwa wofalitsa wina, mkazi kapena mwamuna mnzake. Zilinso choncho ndi mwamuna amene akuphunzira Baibulo ndi mkazi kapena mkazi amene akuphunzira ndi mwamuna.—Mat. 10:16.

Tifunika kusamala pamene tikusankha wina wogwira naye ntchito mu utumiki. Ngakhale kuti ofalitsa, mkazi ndi mwamuna nthaŵi zina angagwire ntchito pamodzi, zimakhala bwino kwambiri ngati ali pagulu. Ngakhale pamene tili mu utumiki, si kwanzeru kutha nthaŵi yaitali tili tokha ndi wina amene sali mkazi wathu kapena mwamuna wathu. Choncho, mbale yemwe akuyang’anira gulu lautumikilo ayenera kusamala pogaŵa ofalitsa, kuphatikizapo achinyamata, kuti agwire ntchito limodzi.

Nthaŵi zonse tikamasamala, tidzapeŵa ‘kudzikhumudwitsa’ tokha kapena anzathu.—2 Akor. 6:3.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena