Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/97 tsamba 1
  • Ikani Zinthu Zofunika Kwambiri Patsogolo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ikani Zinthu Zofunika Kwambiri Patsogolo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Nkhani Yofanana
  • Mitu ya Mabanja—Khalanibe ndi Ndandanda Yabwino Yochitira Zinthu Zauzimu
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kusonkhana?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Mabanja, Tamandani Mulungu Monga Mbali ya Mpingo Wake
    Nsanja ya Olonda—1999
  • Kodi Misonkhano ya Mboni za Yehova Ingakuthandizeni Bwanji?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
km 9/97 tsamba 1

Ikani Zinthu Zofunika Kwambiri Patsogolo

1 Kodi zinthu zina zofunika ndi ziti pa thanzi lathu lauzimu? Ndithudi zimenezi zikuphatikizapo phunziro laumwini, kupezeka pamisonkhano, kupemphera kosalekeza, mayanjano abwino, ndi utumiki wachikristu. Sitingakhale ndi thanzi labwino lauzimu ngati sitiika zinthu zofunika pamalo oyamba m’moyo wathu.

2 Komabe, tonsefe timalimbana ndi zikhumbo zathupi ndipo timafunikiradi kudziletsa. (Agal. 5:17) Tisadzaganize konse kuti tingapindule zambiri mwa kufunafuna zinthu zokonda tokha. (Yer. 17:9) Choncho, ngati tikufuna kutetezera mtima wathu kuti usatisocheretse, tiyenera kumadzipenda nthaŵi zonse.—Miy. 4:23; 2 Akor. 13:5.

3 Pendani Mtima Wanu: Mungadzipende mwa kudzifunsa mafunso oona mtimawa: Kodi ndimalakalaka kuŵerenga Mawu a Mulungu? (1 Pet. 2:2) Kodi ndimazindikira kufunika kwa kupezeka pamisonkhano yonse yampingo? (Aheb. 10:24, 25) Kodi ndimapemphera mosalekeza? (Aroma 12:12) Kodi ndimakonda kucheza ndi anthu okonda zauzimu? (Aroma 1:11, 12) Kodi ndimauona monga udindo wanga, kulengeza uthenga wabwino? (1 Akor. 9:16) Ngati mayankho ali inde, zikusonyeza kuti mumafuna kuika zinthu zofunika kwambiri patsogolo.

4 Pendani Zochita Zanu Zatsiku ndi Tsiku: Mungawonjezere kupenda zokhumba mtima wanuzo mwa kuika zinthu zofunika pamalo oyamba ndi nthaŵi yochitira zimenezo. Zimenezo zikuphatikizapo kukonza ndandanda yoŵerenga Baibulo nthaŵi zonse ndi kope lililonse la Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!, ngakhalenso kukonzekera misonkhano. Muyenera kumapatulanso nthaŵi yophunzira ndi banja ndi kupemphera limodzi. Dziikireni malire a nthaŵi imene mumaonerera TV, ndi imene mumagwiritsira ntchito kompyuta. Tsimikizani kupezeka pamisonkhano yonse yampingo, ndipo pochita zinthu zanu zonse, ikani misonkhano pamalo oyamba. Linganizani kuti banja lonse lizitengamo mbali mu utumiki wakumunda mlungu uliwonse.

5 Mosakayikira, kuika zinthu zofunika kwambiri patsogolo m’moyo wathu kudzatipatsa chimwemwe.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena