CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MASALIMO 119
‘Muzitsatira Chilamulo cha Yehova’
Kutsatira chilamulo cha Yehova kumatanthauza kumvera chilichonse chimene Yehova amatiuza. M’Baibulo muli zitsanzo zambiri za anthu omwe ankadalira Yehova komanso kutsatira chilamulo chake ngati mmene wamasalimo anachitira.
Kutsatira chilamulo cha Yehova n’kumene kumatichititsa kukhalabe osangalala
Yoswa ankadalira kwambiri Yehova akamachita zinthu. Ankadziwa kuti ankayenera kumadalira Yehova ndi mtima wake wonse kuti akhale wosangalala komanso kuti zinthu zizimuyendera bwino
Mawu a Mulungu amatithandiza kuti tikhale olimba mtima tikamakumana ndi mavuto
Yeremiya anali wolimba mtima komanso ankadalira Yehova pamene ankakumana ndi mavuto. Iye ankakhala moyo wosalira zambiri ndipo sanasiye kuchita utumiki wake
Kudziwa bwino Mawu a Mulungu kumatithandiza kuti tizilalikira molimba mtima
Paulo sankachita mantha kulalikira uthenga wochokera kwa Mulungu kwa munthu aliyense. Pamene ankalalikira uthenga wabwino kwa Bwanamkubwa Felike, iye ankakhulupirira kuti Yehova amuthandiza
Kodi ndi pa nthawi iti pamene ndingasonyeze kulimba mtima ndikamalalikira?
Kusukulu
Kuntchito
Achibale
Anthu Ena