Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 June tsamba 5
  • Zimene Tingaphunzire kwa Akhristu Omwe Atumikira kwa Nthawi Yaitali

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Tingaphunzire kwa Akhristu Omwe Atumikira kwa Nthawi Yaitali
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Thandizani Ana Kulidziwa Bwino Gulu la Yehova
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Zinthu Zimene Mungakondwere Nazo
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Khalani Otetezereka m’Gulu Lolinganizidwa la Mulungu
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Tiziphunzira kwa Ofalitsa Aluso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 June tsamba 5
Mlongo wachitsikana wagwira mkono wa mlongo wachikulire.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Zimene Tingaphunzire kwa Akhristu Omwe Atumikira kwa Nthawi Yaitali

M’mipingo yathu tili ndi abale ndi alongo omwe akhala akutumikira Yehova kwa zaka zambiri. Tingaphunzirepo kanthu tikaona mmene asonyezera kudalira Yehova. Tikhoza kuwafunsa zokhudza mbiri ya gulu la Yehova komanso mavuto amene akhala akukumana nawo, ndiponso mmene Yehova wawathandizira kupirira mavutowo. Tikhozanso kuwaitana kuti adzakhale nafe pa Kulambira kwa Pabanja n’cholinga choti adzatifotokozere zimene akhala akukumana nazo pamoyo wawo.

Ngati mwatumikira Yehova kwa nthawi yaitali, muzikhala womasuka kufotokozera achinyamata zomwe mwakumana nazo pa moyo wanu. Yakobo ndi Yosefe ankafotokozera ana awo zimene anakumana nazo pamoyo wawo. (Gen. 48:21, 22; 50:24, 25) Ndipo kenako Yehova anauza mitu ya mabanja kuti iziphunzitsa ana awo zokhudza ntchito zake zazikulu. (Deut. 4:9, 10; Sal. 78:4-7) Masiku anonso, makolo komanso anthu ena mumpingo akhoza kufotokozera achinyamata zinthu zosangalatsa zimene aona Yehova akuchita pogwiritsa ntchito gulu lake.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KUKHALABE OGWIRIZANA PANTHAWI IMENE NTCHITO YATHU INALI YOLETSEDWA, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi ofesi ya nthambi ya ku Austria inathandiza bwanji abale a m’mayiko amene ntchito yathu inali yoletsedwa?

  • Kodi abale a m’mayikowa anachita zotani kuti chikhulupiriro chawo chikhalebe cholimba?

  • N’chifukwa chiyani ofalitsa ambiri a ku Romania anachoka m’gulu la Yehova, nanga anabwerera bwanji?

  • Kodi zimene abalewa anakumana nazo zalimbitsa bwanji chikhulupiriro chanu?

Zithunzi zomwe zili mu vidiyo yakuti ‘Kukhalabe Ogwirizana Panthawi Imene Ntchito Yathu Inali Yoletsedwa.’ 1. Mapu osonyeza mayiko omwe ntchito yathu inali yoletsedwa Kum’mawa kwa Europe. 2. Mashini osindikizira. 3. Abale a ku Romania akumbatirana.

Akhristu omwe atumikira kwa nthawi yaitali angakulimbikitseni mwauzimu

Koma bwanji ngati ofalitsa ambiri a mumpingo mwanu abatizidwa chaposachedwapa? Mukhoza kupeza nkhani za Akhristu omwe atumikira kwa zaka zambiri pa jw.org pagawo lakuti Laibulale pa mbali yakuti “Mavidiyo” kapena mukhoza kupeza nkhani zina mu Watch Tower Publications Index pagawo lakuti “Life Stories of Jehovah’s Witnesses.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena