Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb24 May tsamba 12-13
  • June 17-23

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • June 17-23
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2024
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2024
mwb24 May tsamba 12-13

JUNE 17-23

MASALIMO 51-53

Nyimbo Na. 89 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kodi Mungatani Kuti Mupewe Kuchita Machimo Akuluakulu?

(10 min.)

Musamadzidalire; munthu aliyense akhoza kulakwitsa (Sl 51:5; 2Ak 11:3)

Muzichita zimene zingakuthandizeni kukhala pa ubwenzi wabwino kwambiri ndi Yehova (Sl 51:6; w19.01 15 ¶4-5)

Muziyesetsa kuti musamalakelake kapena kuganizira zinthu zoipa (Sl 51:10-12; w15 6/15 14 ¶5-6)

Zithunzi zosonyeza m’bale wachinyamata akuchita zinthu zokhudza kulambira. 1. Akuwerenga Baibulo. 2. Akupemphera kuchokera pansi pa mtima. 3. Akuyankha pa misonkhano. 4. Akulalikira pogwiritsa ntchito shelefu.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Sl 52:2-4​—Kodi lembali likufotokoza zotani zokhudza Doegi? (it-1 644)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Sl 51:1-19 (th phunziro 12)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. (lmd phunziro 7 mfundo 3)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. (lmd phunziro 4 mfundo 4)

6. Ulendo Wobwereza

(3 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. M’phunzitseni za dzina la Mulungu. (lmd phunziro 9 mfundo 5)

7. Kuphunzitsa Anthu

(4 min.) lff phunziro 14 mfundo 7 ndi Zimene Ena Amanena (lmd phunziro 11 mfundo 5)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 115

8. Zomwe Mungachite Kuti Mukonze Zomwe Mwalakwitsa

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Zithunzi za muvidiyo yakuti “Moyo Wanga Wachinyamata​—Ndingatani Kuti Ndikonze Zomwe Ndinalakwitsa M’mbuyo?” 1. Thalila. 2. José.

Ngakhale titayesetsa bwanji, tonsefe timalakwitsa zinthu zina. (1Yo 1:8) Ndiye zikachitika, tisamalole kuti manyazi kapena mantha atilepheretse kubwerera kwa Yehova kuti atikhululukire komanso atithandize. (1Yo 1:9) Nthawi zonse kupemphera kwa Yehova kumakhala chinthu choyamba chomwe munthu angachite kuti akonze zomwe walakwitsa.

Werengani Salimo 51:1, 2, 17. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi mawu a Davidewa angatilimbikitse bwanji kubwerera kwa Yehova kuti atithandize pamene tachita tchimo lalikulu?

Onerani VIDIYO yakuti Moyo Wanga Wachinyamata​—Ndingatani Kuti Ndikonze Zomwe Ndinalakwitsa M’mbuyo? Kenako funsani omvera mafunso otsatirawa:

  • Kodi ndi zinthu ziti zomwe zinachititsa Thalila ndi José kuti alakwitse zinthu?

  • Kodi anachita zotani kuti akonze zimene analakwitsazo?

  • Kodi kuchita zimenezo kunawathandiza bwanji?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 11 ¶5-10, bokosi patsamba 89

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 129 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena