Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb26 January tsamba 14-16
  • February 23–March 1

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • February 23–March 1
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
mwb26 January tsamba 14-16

FEBRUARY 23–MARCH 1

YESAYA 38-40

Nyimbo Na. 4 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

M’busa wakumbatira kamwana ka nkhosa.

M’busa wa m’nthawi ya Aisiraeli wanyamula nkhosa mwachikondi pachifuwa chake

1. “Iye Adzasamalira Gulu la Nkhosa Zake Ngati Mʼbusa”

(10 min.)

Yehova wapereka komanso kuteteza Mawu ake, Baibulo, kuti tikhale naye pa ubwenzi (Yes 40:8; w23.02 2-3 ¶3-4)

Iye amatisamalira mwachikondi (Yes 40:11; cl 70 ¶7-mwbr)

Amatidziwa aliyense payekha komanso kutithandiza kupirira mavuto athu (Yes 40:​26-29; w18.01 8 ¶4-6)

Akulu awiri apita kunyumba kwa mlongo yemwe ali ndi ana awiri kuti akacheze nawo.

FUNSO LOFUNIKA KULIGANIZIRA: Kodi zimene lemba la Yesaya 40:11 limafotokoza zokhudza m’busa, zimakhudza bwanji mmene mumaonera Yehova?

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 40:3—Kodi mawu a palembali anakwaniritsidwa bwanji Yesu asanayambe utumiki wake padzikoli? (ip-1 400 ¶7)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 40:​21-31 (th phunziro 11)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Pezani mpata wofotokozera munthu mfundo inayake imene mwaphunzira pamisonkhano posachedwapa. (lmd phunziro 4, mfundo 3)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Pezani mpata wofotokozera munthu mfundo inayake imene mwaphunzira pamisonkhano posachedwapa. (lmd phunziro 4, mfundo 4)

6. Ulendo Wobwereza

(2 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. (lmd phunziro 7, mfundo 5)

7. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) lff phunziro 18 zomwe taphunzira, kubwereza, komanso zolinga. Gwiritsani ntchito nkhani imene ili pagawo lakuti “Onani Zinanso” pothandiza wophunzira wanu kumvetsa chikondi chimene a Mboni za Yehova amasonyezana. (lmd phunziro 11, mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 160

8. Lipoti la Chaka cha Utumiki

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Pambuyo powerenga chilengezo chochokera ku ofesi ya nthambi chokhudza lipoti la chaka cha utumiki, funsani omvetsera kuti afotokoze zinthu zabwino zomwe zili mu Lipoti la Chaka cha Utumiki cha 2025 la Mboni za Yehova Padziko Lonse. Funsani ofalitsa omwe munawasankhiratu kuti afotokoze zinthu zolimbikitsa zimene anakumana nazo mu utumiki chaka chathachi.

Zithunzi: Abale ndi alongo padziko lonse akugwira ntchito yolalikira. 1. Mlongo akuphunzira Baibulo ndi mzimayi pogwiritsa ntchito buku la “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale.” 2. Banja likuwerengera Baibulo bambo wina pomwe likulalikira nyumba ndi nyumba. 3. Mlongo akulalikira mzimayi. 4. Banja likuwerengera Baibulo mayi wina pomwe likulalikira nyumba ndi nyumba. 5. Banja likuphunzira Baibulo ndi bambo wina pogwiritsa ntchito kabuku kakuti “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale.” 6. Mlongo akuonetsa mayi wina vidiyo. 7. Banja likulalikira mayi wina pogwiritsa ntchito chinenero cha manja ndipo likumuonetsa vidiyo.

Based on NASA/Visible Earth imagery

Mu 2025, anthu a Yehova anapitiriza kuchita khama polalikira kunyumba ndi nyumba komanso kuchititsa maphunziro a Baibulo

  • Kodi ndi zinthu zosangalatsa ziti zokhudza Lipoti la Chaka cha Utumiki cha 2025 zimene mungakonde kufotokoza?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 64-65

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 161 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena