Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb26 March tsamba 6-7
  • March 23-29

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • March 23-29
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
mwb26 March tsamba 6-7

MARCH 23-29

YESAYA 48-49

Nyimbo Na. 89 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Mukamamvera Yehova Zinthu Zidzakuyenderani Bwino

(10 min.)

Yehova amaphunzitsa atumiki ake (Yes 48:17; it-E “Mphunzitsi, Kuphunzitsa” ¶2-mwbr)

Timafunika kusankha kumvera Yehova (Yes 48:18a; ijwbq nkhani na. 44 ¶2-3-mwbr)

Tikatero mtendere wathu udzakhala “ngati mtsinje” ndipo chilungamo chathu chidzakhala “ngati mafunde a mʼnyanja” (Yes 48:18b; lv 199 ¶8-mwbr)

Mlongo akuyenda m’mbali mwa nyanja pamene dzuwa likulowa.

TANTHAUZO: Mawu a Chiheberi omwe anawamasulira kuti “mtendere” anganenenso za thanzi, chitetezo, mphamvu, moyo wabwino, ubwenzi kapenanso kukwanira bwino.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 49:8—Kodi ulosiwu unakwaniritsidwa m’njira zitatu ziti? (it-E “Nthawi Yovomerezeka” ¶1-3-mwbr)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 48:​9-20 (th phunziro 11)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Itanirani wachibale yemwe anasiya kusonkhana ku nkhani yapadera komanso ku Chikumbutso. (lmd phunziro 5, mfundo 3)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Fotokozerani munthu yemwe akufuna kukapezeka ku Chikumbutso zokhudza zimene zikachitike. (lmd phunziro 9, mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(5 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Pambuyo pa nkhani ya Chikumbutso, yankhani mafunso a munthu wachidwi yemwe anapezekapo. (lmd phunziro 8, mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 107

7. Zimene Mungachite Kuti Mudzapindule pa Tsiku Lofunika Kwambiri pa Chaka

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Tikamapezeka pa Chikumbutso chaka chilichonse timasonyeza kuti timamvera lamulo la Yesu komanso timayamikira Yehova chifukwa cha mphatso ya dipo. (Lu 22:19) Komabe mwambowu umatikumbutsanso kuti Yehova ndi Mwana wake amatikonda kwambiri. (Aga 2:20; 1Yo 4:​9, 10) Kodi tingatani kuti tidzapindule kwambiri ndi mphatso imene Yehova anatipatsayi? Kodi tingathandize bwanji ena kuti nawonso adzapindule?

  • Kuyamba kuwerenga Baibulo panyengo ya Chikumbutso tsiku lililonse

  • Kuganizira mphatso ya dipo komanso kuchita zinthu m’njira yosonyeza kuti timaliyamikira

  • Kuchita zonse zomwe tingathe kuti tiitanire anzathu, achibale ndi anthu a m’gawo lathu ku nkhani yapadera komanso mwambo wa Chikumbutso

  • Kulandira anthu amene abwera ku Chikumbutso mwansangala. Kuwonjezera pa kuchita chidwi ndi anthu amene inuyo munawaitanira, muzidzachitanso chidwi ndi anthu ena omwe abwera, ndipo ngati n’kotheka mudzakhale nawo limodzi

  • Mudzakhale okonzeka kuyankha mafunso a alendo omwe abwera

  • Mudzakhale okonzeka kulandira anthu amene anasiya kusonkhana. Makamaka akulu adzakhale tcheru kulandira omwe anachotsedwa

Chithunzi cha muvidiyo yakuti: “Yesu “Anabwera Kudzafunafuna Ndi Kupulumutsa Anthu Osochera.”” Abale ndi alongo akucheza mosangalala m’Nyumba ya Ufumu pa tsiku la Chikumbutso.

Onerani VIDIYO yakuti Yesu “Anabwera Kudzafunafuna Ndi Kupulumutsa Anthu Osochera.” Kenako funsani funso ili:

  • Kodi mwaphunzira chiyani pa nkhani yolandira anthu amene anafooka omwe adzabwere ku Chikumbutso?

    Chithunzi cha muvidiyo yakuti: “Yesu “Anabwera Kudzafunafuna Ndi Kupulumutsa Anthu Osochera.”” Mlongo amene anasiya kusonkhana wafika pa Chikumbutso ndipo mlongo wina akumuhaga mwachikondi.

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 72-73

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 134 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena