Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb26 March tsamba 4-5
  • March 16-22

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • March 16-22
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
mwb26 March tsamba 4-5

MARCH 16-22

YESAYA 45-47

Nyimbo Na. 2 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. “Ine Ndine Mulungu Ndipo Palibe Aliyense Wofanana ndi Ine”

(10 min.)

Gulu la Aisraeli omwe anagwidwa ukapolo likutuluka mumzinda wa Babulo.

Palibe aliyense wofanana ndi Yehova (Yes 46:9; w20.06 5 ¶14-mwbr)

Palibe chimene chingalepheretse Yehova kukwaniritsa cholinga chake (Yes 46:10, 11; cl 42 ¶14-mwbr; it-E “Ayuda Omwe Anali ku Ukapolo ku Babulo Anabwerera Kwawo” ¶1-mwbr)

Anthu amene amadalira milungu yabodza ndi amene amagwiritsidwa fuwa lamoto (Yes 46:6, 7; w99 5/15 14 ¶18-19-mwbr)

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 46:10—Kodi Yehova anadziwiratu pachiyambi kuti Adamu ndi Hava adzachimwa? (w11 1/1 14 ¶2-3-mwbr)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 45:​1-11 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Fotokozerani munthu yemwe si Mkhristu zimene zimachitika pamwambo wa Chikumbutso. (lmd phunziro 5, mfundo 3)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Pemphani munthu amene pa ulendo wapita analandira kapepala koitanira anthu ku Chikumbutso kuti muziphunzira naye Baibulo. (lmd phunziro 9, mfundo 5)

6. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) lff phunziro 19 mawu oyamba ndi mfundo 1-3 (lmd phunziro 11, mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 38

7. Amene Tingamudalire Kuti Azitithandiza

(7 min.) Nkhani yokambirana.

Tikakumana ndi mavuto, tizidalira Mulungu wathu Yehova kuti azitithandiza.—Ahe 13:​5, 6.

Werengani Salimo 55:22. Kenako kambiranani zitsanzo zotsatirazi ndi omvetsera.

Zithunzi: Abale ndi alongo akukumana ndi mavuto osiyanasiyana. 1. M’bale amene ali ndi nkhawa kwambiri chifukwa choti ntchito yamuthera, wakhala pamasitepesi. 2. M’bale amene ali m’ndende akufunsidwa mafunso ndi apolisi. 3. Mlongo akupemphera chamumtima, kupempherera mwamuna wake amene akudwala. 4. Mwamuna ndi mkazi wake amene apulumuka pangozi ya m’chilengedwe akuoneka odandaula.

Pa chitsanzo chilichonse, lembani njira imodzi yomwe tingasonyezere kuti timadalira Yehova komanso imene iye amatithandizira.

  • Atichotsa ntchito kapena tikuvutika kupeza ndalama zosamalira banja lathu

  • Akuluakulu a boma aletsa ntchito yathu

  • Tikudwala matenda aakulu

  • Takumana ndi vuto lalikulu monga ngozi ya m’chilengedwe kapena imfa ya munthu amene timamukonda

8. Lipoti la Dipatimenti Yoona za Mapulani ndi Zomangamanga la 2026

(8 min.) Nkhani.

Onerani VIDIYOYI.

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 70-71

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 148 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena