Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w25 September tsamba 32
  • Yesu “Anaphunzira Kumvera”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu “Anaphunzira Kumvera”
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • “Anaphunzira Kumvera”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
  • Phunzirani Kumvera Mwakulandira Chilango
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Kodi Muli ndi “Mtima Womvera”?
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Kumvera—Kodi Ndi Phunziro Lofunika Paubwana?
    Nsanja ya Olonda—2001
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
w25 September tsamba 32

MAWU A M’BAIBULO

Yesu “Anaphunzira Kumvera”

Yesu wakhala akumvera Yehova kuyambira kalekale. (Yoh. 8:29) Ndiye n’chifukwa chiyani Baibulo limanena kuti: Iye “anaphunzira kumvera chifukwa cha mavuto amene anakumana nawo”?—Aheb. 5:8.

Yesu ali padzikoli anakumana ndi zinthu zomwe sizinkachitika kumwamba. Mwachitsanzo, analeredwa ndi makolo oopa Mulungu koma sanali angwiro. (Luka 2:51) Anazunzidwanso ndi atsogoleri a chipembedzo achinyengo komanso olamulira opanda chilungamo. (Mat. 26:59; Maliko 15:15) Komabe iye “anadzichepetsa ndipo anakhala womvera mpaka imfa,” yomwe inali yowawa kwambiri.—Afil. 2:8.

Zimenezi zinachititsa kuti Yesu aphunzire kumvera m’njira imene siikanatheka ali kumwamba. Choncho anakhala Mfumu komanso Mkulu wa Ansembe wabwino kwambiri, yemwe akhoza kutimvetsa. (Aheb. 4:15; 5:9) Yesu anakhala wamtengo wapatali kwambiri kwa Yehova ataphunzira kumvera chifukwa cha mavuto amene anakumana nawo. Ifenso tingakhale amtengo wapatali kwambiri kwa Yehova ndipo angatigwiritsire ntchito pa utumiki uliwonse ngati titakhalabe omvera ngakhale pamene takumana ndi mavuto.—Yak. 1:4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena