Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w25 November tsamba 32
  • Muzigwiritsa Ntchito ‘Mphatso Yanu ya Uzimu’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzigwiritsa Ntchito ‘Mphatso Yanu ya Uzimu’
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • Tipitirize Kulimbikitsana Tsiku ndi Tsiku
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Zimene Mungachite Kuti Mphatso Ikhale Yabwino Kwambiri
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • N’chifukwa Chiyani Mphatso Imene Mulungu Watipatsa Ndi Yamtengo Wapatali?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Mphatso yachikoka—Kodi Munthu Atamandidwe Kapena Mulungu Alemekezedwe?
    Nsanja ya Olonda—1998
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
w25 November tsamba 32

MAWU A M’BAIBULO

Muzigwiritsa Ntchito ‘Mphatso Yanu ya Uzimu’

Tonsefe timasangalala tikamalimbikitsana ndi abale komanso alongo athu. Koma kuti tilimbikitsane, tikufunika kuchita zambiri kuposa kungokhala ndi abale komanso alongo athu. Baibulo limanena kuti mwayi umene tili nawo wolimbikitsana ndi ‘mphatso yauzimu.’ (Aroma 1:​11, 12) Kodi tingatani kuti tizigwiritsa ntchito mphatso imeneyi mokwanira?

Zolankhula zanu zizilimbikitsa anthu ena. Mwachitsanzo, tingapereke ndemanga kumisonkhano zimene zingapangitse anthu kuti aziganizira za Yehova, Mawu ake komanso anthu ake, osati za ifeyo. Tikamacheza ndi abale komanso alongo athu, tingachite bwino kumakambirana nkhani zolimbikitsa.

Zosankha ndi zochita zanu zizilimbikitsa anthu ena. Mwachitsanzo, anthu ena amasankha kupitiriza kuchita utumiki wa nthawi zonse ngakhale kuti akukumana ndi mavuto. Ena amapezeka pa misonkhano ya m’kati mwa mlungu nthawi zonse ngakhale kuti amapanikizika ndi ntchito kapena ali ndi matenda okhalitsa.

Kodi zimene mumalankhula komanso kuchita zimalimbikitsa abale ndi alongo anu? Kodi mumaona zimene abale ndi alongo anu amalankhula komanso kuchita pofuna kukulimbikitsani?

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena