Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 13
  • Kodi Nkhani Zokhudza Moyo wa Yesu Zinalembedwa Liti?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Nkhani Zokhudza Moyo wa Yesu Zinalembedwa Liti?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Kodi Kwenikweni Uthenga Wabwino Nchiyani?
    Nsanja ya Olonda—1992
  • “Chipangano Chatsopano”—Mbiri Yeniyeni Kapena Nthano?
    Baibulo—Kodi Ndilo Mawu a Mulungu Kapena a Munthu?
  • Choonadi Ponena za Yesu
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Kodi Baibulo Limafotokoza Zonse Zokhudza Yesu?
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 13
Munthu akulemba mumpukutu

Kodi Nkhani Zokhudza Moyo wa Yesu Zinalembedwa Liti?

Yankho la m’Baibulo

Ponena za nkhani imene analemba yokhudza moyo wa Yesu, mtumwi Yohane anati: “Munthu amene anaona zimenezo akuchitira umboni, ndipo umboni wakewo ndi woona. Munthu ameneyu akudziwa kuti amanena zoona, kuti inunso mukhulupirire.”—Yohane 19:35.

Pali chifukwa chinanso chimene tiyenera kukhulupirira nkhani za m’mabuku a Uthenga Wabwino zimene zinalembedwa ndi Mateyu, Maliko, Luka ndi Yohane. Chifukwa chake n’chakuti iwo analemba nkhanizo pa nthawi imene anthu ambiri omwe anaona ndi maso zimene analembazo, anali adakali moyo. Malinga ndi maumboni ena, buku la Uthenga Wabwino la Mateyu linalembedwa mu 41 C.E., patangopita zaka 8 zokha kuchokera pamene Khristu anamwalira. Akatswiri ena a Baibulo amati bukuli linalembedwa nthawi ina m’tsogolo. Komabe, pafupifupi akatswiri onse a Baibulo amavomereza kuti mabuku onse a Malemba Achigiriki (Chipangano Chatsopano) analembedwa m’nthawi ya atumwi.

Panali anthu ambiri omwe analipo pamene Yesu anali ndi moyo padziko lapansi, pa nthawi imene anaphedwa ndiponso pamene anaukitsidwa. Anthu amenewa akanatha kutsutsa nkhani za m’mabuku a Uthenga Wabwino zikanakhala kuti nkhanizo sizinali zolondola. Mwachitsanzo, pulofesa Frederick F. Bruce ananena kuti: “Umboni wamphamvu pa nkhani imeneyi ndi zimene atumwi ananena polalikira. Iwo ankadziwa zoti anthu amene ankamvetserawo ankadziwanso zinthu zokhudza Yesu zimene atumwiwo ankalalikira. N’chifukwa chake iwo atanena kuti ‘ife ndife mboni za choonadi chimenechi,’ ananenanso kuti ‘monga mmene inunso mukudziwira’ (Machitidwe 2:22).”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena