Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g88 9/8 tsamba 27
  • Pompi Yodabwitsa ya Mtengo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pompi Yodabwitsa ya Mtengo
  • Galamukani!—1988
  • Nkhani Yofanana
  • Kumene Kuli Mavuto Aakulu
    Galamukani!—1997
  • “Mtengo wa Moyo” Wodabwitsa wa Afirika
    Galamukani!—1995
  • Kodi Padzikoli Madzi Akutha?
    Galamukani!—2001
  • Madzi Opatsa Moyo Wosatha
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Galamukani!—1988
g88 9/8 tsamba 27

Pompi Yodabwitsa ya Mtengo

Masamba omwe ali m’mwamba mu mtengo amafunikira madzi ndi zakudya, kaŵirikaŵiri zikwi za magaloni pa tsiku. Awa amafunikira kukwezedwa m’mwamba, koma motani?

“Kutulutsa madzi kozizwitsa kumeneku kumayambira pansi mu nthaka kumene mamiliyoni a zidutswa zazing’ono za mizu zimasonkhanitsa madzi ndi zakudya zofunika zosungunulidwa,” ikulongosola tero Compressed Air Magazine. “Pamene madzi akugwiritsiridwa ntchito, kusoweka kumapangidwa m’masamba komwe kumapangitsa zofunikazo kukwera m’mwamba ndipo m’chenicheni kukoka madzi owonjezereka kuchokera mu nthaka. Palibe makina operekera madzi opangidwa ndi munthu omwe angapereke madzi kuposa pa chifupifupi mamita 10.” Koma bwanji ponena za dongosolo la kupereka madzi la mtengo?

Liri lozizwitsa kwambiri kotero kuti kwanenedwa kuti lingakhoze, ngati kuli koyenerera, kupereka madzi mu mtengo kwa chifupifupi makilomita atatu m’mwamba! Nchosadabwitsa kuti kusatsa malonda kochitidwa ndi kampani yopanga mapompi yotchuka kumakokera chisamaliro ku “pompi yozizwitsa” ya mtengo wa maple ndipo imavomereza kuti: “Sitingalingane ndi chilengedwe m’kuleza mtima kapena kachitidwe.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena