Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g91 10/8 tsamba 31
  • Kuganiza kwa Nyani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuganiza kwa Nyani
  • Galamukani!—1991
  • Nkhani Yofanana
  • Phunziro 2
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
  • Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Ana ‘Pa Ngongole’—Kodi Kachitidweko Kali Kanzeru Motani?
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Ntchito Yopanga Ophunzira Yakhudza Kwambiri Zochita Pamoyo Wanga
    Nsanja ya Olonda—2007
Onani Zambiri
Galamukani!—1991
g91 10/8 tsamba 31

Kuganiza kwa Nyani

Mu Sierra Leone, Kumadzulo kwa Afirika, kuli mwambi wakuti: “Nyani samangowuza mwana wake kuti, ‘Gwiritsa!’ Amanena kuti, ‘Dziyang’ana pansi.’”

Izi zimatipangitsa kulingalira chithunzi cha nyani wamng’ono ali m’mwamba mumtengo, akumamatira kumsana kwa mayi ŵake. Tanthauzo la mwambiwo nlakuti ngati Amayi angonena kuti gwiritsa, mwana ŵake angatero kwakanthaŵi, koma popeza kuti sakudziŵa chifukwa cha lamulolo, angaiwale mwamsanga ndikutairira.

Komabe, ngati mwanayo akuyang’ana pansi, angawone mtunda womwe ulipo kuchokera pansi ndipo angatsimikiziridwe mwamphamvu kuti moyo wake ukuloŵetsedwamo. Mwachitsanzo, iye angavulazidwe moipa kapena ngakhale kufa kumene! Pokhala atamvetsetsa ngoziyo mokwanira, amakhala ndi chisonkhezero champhamvu chogwirira zolimba. Tsopano chenjezo kapena lamulo lina lirilonse lowonjezeredwa lidzalemekezedwa kwenikweni.

Ha, ndilamulo lamakhalidwe abwino lotani nanga lophunzitsira ena, makamaka ana. Phunziro lothandiza la nkhaniyi nlakuti m’malo mongopereka malamulo, kuli kofunika kumpangitsa kuzindikira.

Ndithudi, pazochitika zina sipangakhale nthaŵi yokwanira kuchita zimenezo poyamba. Mwachitsanzo, ngati mwana wanu ayamba kudutsa msewu wokhala ndi magalimoto ambiri popanda kuyang’ana choyamba, mungamulamule kuima ndikubwerera mofulumira. Kupereka lamuloli choyamba panopa kuli kofunika koposa. Komano kufotokoza ngozi yomwe mwanayo analimo kungampangitse kuzindikira.

Phindu la kachitidwe kameneka—kusangopereka lamulo komanso kumpangitsa kuzindikira—likupezeka m’mwambi wa m’Baibulo uwu: ‘Wosunga chilamulo ndiye mwana wozindikira.’—Miyambo 28:7.

[Mawu a Chithunzi patsamba 31]

© Zoological Society of San Diego

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena