Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g03 2/8 tsamba 17
  • Ubwino wa Kumwetulira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ubwino wa Kumwetulira
  • Galamukani!—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Mwetulirani—N’zothandiza kwa Inu!
    Galamukani!—2000
  • Kumwetulira Ndi Mphatso Yofunika Kugawana
    Galamukani!—2017
  • Phunziro 5
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2005
Onani Zambiri
Galamukani!—2003
g03 2/8 tsamba 17

Ubwino wa Kumwetulira

NGAKHALE kuti chinthu chimenechi chimachitika kwa nthaŵi yochepa, munthu angathe kuchikumbukira moyo wake wonse. N’chinthu chamtengo wapatali kwambiri, koma palibe munthu amene ali wosauka kwambiri moti sangachikwanitse kapena amene ali wolemera kwambiri moti sachifuna. Kodi tikunena za chiyani? Tikunena za kumwetulira.

Kuti munthu amwetulire chimachitika n’chakuti milomo imakokeka n’kumanyevukira m’mwamba ndipo zimenezi zimakhudzanso maso ake. Munthuyo amatero akasangalala ndi chinachake. Khanda limayamba kumwetulira pakatha milungu ingapo litabadwa, ndipotu zimenezi makolo ake amasangalala nazo. Uku sikukhala kumwetulira kochita kufuna. Akatswiri amanena kuti kumwetulira kotere kumakonda kuchitika khanda likamalota ndipo mwina n’chifukwa cha zimene zimachitika m’maganizo ndiponso mu ubongo wake. Ndipo ngakhale tikakula, timathabe kumwetulira motere tikamaphwetsa mkhuto kapena tikamamvetsera nyimbo.

Komano kamwana kakatha mwezi umodzi ndi theka, kamamwetulira chifukwa choti kaona munthu kapena kamva mawu enaake. Inde, ana ndi akulu omwe amamva bwino akamamwetulirana mochita kufuna. Akuti kumwetulira kotere kumathandiza kuti tikhale athanzi. Mirtha Manno ndi Rubén Delauro, madokotala othandiza anthu ovutika kuyankhula, amenenso ali ndi chipatala chophunzitsirapo anthu za phindu la kumwetulira chotchedwa Smiling and Health, anati kumwetulira pakokha kumachititsa thupi kutulutsa madzi enaake opita ku ubongo ndipo zikatere ifeyo timamva bwino.

Kumwetulira n’kofunikanso chifukwa ena amapindulanso nako. Tikamwetulira mochokadi pansi pamtima, kaya pokumana ndi munthu, posonyeza kumvera mnzathu chifundo, kapenanso polimbikitsa ena, anthu amatha kuona mmene tikumvera ngakhale titapanda kunena chilichonse. Nthaŵi zina, kungoona chithunzi cha mwana akumwetulira mochititsa kaso kungachititse kuti ifenso timwetulire.

Tingathe kukhala omasuka, mtima wathu ungazizire komanso tingapirire zovuta zinazake munthu winawake akangotiyang’ana n’kumamwetulira. Baibulo limati: “Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.” (Miyambo 3:27) Inde, kumwetulira komweku, tingapindule nako ndiponso tingapindulitse nako ena. Bwanji osayesetsa kugwiritsira ntchito bwino mphatso yamtengo wapatali kwambiri imeneyi ya kumwetulira mochoka pansi pamtima?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena