Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 8/14 tsamba 7
  • Zochitika Padzikoli

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zochitika Padzikoli
  • Galamukani!—2014
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Padziko Lonse
  • Britain
  • Russia
  • Africa
  • United States
  • Mpweya
    Galamukani!—2023
  • Zinthu Zachilengedwe Zikutha Padziko Pano
    Galamukani!—2005
  • Kodi Munthu Akuchitanji ndi Dziko Lapansi?
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Kuipitsa Kodi Ndani Akukuchititsa?
    Galamukani!—1990
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 8/14 tsamba 7

ZOCHITIKA PADZIKOLI

Padziko Lonse

Mwana wamng’ono

Bungwe lina loona za umoyo wa ana linanena kuti: “Chaka chilichonse ana pafupifupi 3 miliyoni amamwalira asanakwanitse mwezi umodzi, ndipo ambiri mwa anawa amamwalira pa zifukwa zopeweka. Ana oposa 1 miliyoni pa ana amenewa, amamwalira tsiku lomwe abadwa.”

Britain

Munthu akuthira dizilo m’thanki ya galimoto

Bungwe lina la za umoyo ku England linanena kuti mu 2011, chiwerengero cha anthu omwalira chifukwa chopuma mpweya woipa chinawonjezeka m’matauni 15 a mumzinda wa London. Ena amati dizilo ndi wosaopsa kwambiri ku thanzi la anthu chifukwa satulutsa mpweya wambiri woipa. Komabe anthu ambiri amene anafa m’matauni amenewa, anafa chifukwa cha utsi wochokera m’magalimoto oyendera dizilo.

Russia

Kafukufuku amene bungwe lina la ku Russia linachita mu 2013 anasonyeza kuti Akhristu 52 pa 100 alionse a mpingo wa Orthodox m’dzikoli, sanawerengepo Baibulo. Kafukufukuyu anasonyezanso kuti Akhristu 28 pa 100 alionse amangopemphera mwa apo ndi apo.

Africa

Mlimi wa ku Africa

Lipoti la banki lalikulu padziko lonse linanena kuti kukanganirana malo olima kukuchititsa kuti ulimi usamayende bwino. Izi zikuchititsanso kuti umphawi uziwonjezeka. Hafu ya malo omwe sakulimidwa padziko lonse, yomwe ndi maekala 500 miliyoni, ali ku Africa. Koma kumeneku n’kumenenso kuli nthaka yabwino moti malo amenewa akanakhala kuti akulimidwa, bwenzi akutulutsa chakudya chambiri.

United States

Tabuleti komanso mulu wa mabuku a kusukulu

Sukulu ndi yunivesite zambiri zasiya kugwiritsa ntchito mabuku ndipo zikumagwiritsa ntchito matabuleti. Ana a sukulu akumatha kuwerenga komanso kumvetsera ndi kuonera zinthu za kusukulu pogwiritsa ntchito matabuletiwa. Komabe anthu ena akukayikira ngati njirayi ili yotchipa kuyerekeza ndi kugwiritsa ntchito mabuku.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena