Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 1/15 tsamba 16
  • Zipembedzo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zipembedzo
  • Galamukani!—2015
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Padziko Lonse
  • England
  • Australia
  • Kodi Ndingachidziwe Bwanji Chipembedzo Cholondola?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Chipembedzo Chirichonse Chiri Chabwinodi?
    Nsanja ya Olonda—1991
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Akusiya Zipembedzo Zawo?
    Galamukani!—2015
  • Kulondola Chipembedzo Choyera Kaamba ka Chipulumutso
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Galamukani!—2015
g 1/15 tsamba 16
Denga la tchalitchi

ZOCHITIKA PADZIKOLI

Zipembedzo

Zipembedzo ziyenera kuthandiza anthu kukhala ogwirizana. Koma n’zomvetsa chisoni kuti zipembedzo zimapangitsa kuti anthu azikangana komanso kuti asamakhulupirirane.

Padziko Lonse

Chithunzi chosonyeza mbali yaikulu ya dziko lapansi

Anthu ambiri amakhala m’mayiko omwe muli malamulo okhwima okhudza zipembedzo. Malamulowa anawakhazikitsa chifukwa cha mfundo zandale komanso chifukwa cha kusagwirizana kwa anthu. M’zaka 5 zapitazi, chiwerengero cha mayiko amene anthu ake amazunzidwa chifukwa choti ali m’zipembedzo za anthu ochepa, chinawonjezeka kwambiri.

TAGANIZIRANI IZI: Kodi ndi zinthu ziti zomwe zimapangitsa anthu ena kuti azidana ndi zipembedzo?—Mateyu 23:27, 28; Yohane 15:19.

England

A Tony Blair omwe anali nduna yaikulu ku England analemba m’nyuzipepala ina kuti zinthu zambiri zomwe zigawenga zikuchita, “zikuchitika m’dzina la chipembedzo. Nkhondo zambiri zimene zikuchitika m’zaka za m’ma 2000 zino, siziyamba pa zifukwa zandale ngati mmene zinalili m’ma 1900. Zambiri zikuchitika chifukwa cha kusagwirizana pa nkhani za chikhalidwe komanso zipembedzo.”—Observer.

TAGANIZIRANI IZI: N’chifukwa chiyani nthawi zambiri zipembedzo zimapangitsa kuti anthu asamagwirizane?—Maliko 7:6-8.

Australia

Chithunzi chosonyeza munthu m’modzi yemwe wakhwatchidwa ndipo ena 4 aimika manja

Kafukufuku wina anasonyeza kuti ku Australia, munthu mmodzi pa 5 alionse amanena kuti alibe chipembedzo. Komanso “anthu ambiri amene ali ndi chipembedzo, sapitako nthawi zonse komanso sachita nawo zinthu zambiri zokhudza chipembedzo chawocho.” Kafukufukuyu anasonyeza kuti amuna 15 okha pa 100 alionse komanso akazi 22 okha pa 100 alionse, ndi amene amalimbikira kuchita nawo zonse zokhudza chipembedzo chawo.

TAGANIZIRANI IZI: Kodi ndi makhalidwe ati oipa omwe anthu azipembedzo zambiri amachita?—Mateyu 7:15-20.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena