Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g25 No. 1 tsamba 12-13
  • Muzikhala Wopatsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzikhala Wopatsa
  • Galamukani!—2025
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?
  • ZIMENE MUNGACHITE
  • Anthu Opatsa Amakhala Osangalala
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • N’chifukwa Chiyani Ndikufunika Kumathandiza Ena?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Yehova Ndi Wowolowa Manja Ndiponso Wololera
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Malangizo Otithandiza Kukhala Mwamtendere Ndi Anzathu
    Galamukani!—2021
Onani Zambiri
Galamukani!—2025
g25 No. 1 tsamba 12-13
Banja losauka likudya mosangalala ndi mlendo.

ZIMENE MUNGACHITE PA VUTO LA KUKWERA MITENGO KWA ZINTHU

Muzikhala Wopatsa

Ngati mukuvutika chifukwa cha kukwera mitengo kwa zinthu, mukhoza kuganiza kuti simungakhale wopatsa. Koma kukhala wopatsa kungakuthandizeni kuti musamavutike kwambiri ndi vuto la kukwera mitengo. N’zotheka ndithu kukhala wopatsa koma osawononga ndalama.

N’CHIFUKWA CHIYANI KUCHITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA?

Kukhala wopatsa, ngakhale pa zinthu zing’onozing’ono, kumatithandiza kukhala wosangalala komanso kuti tisamadzikayikire. Ndipotu kafukufuku amasonyeza kuti kukhala wopatsa kumathandiza kuti tikhale ndi moyo wathanzi komanso tiziganiza bwino. Mwachitsanzo, zimathandiza kuti tisamade nkhawa, BP isakwere komanso tisamamve kuphwanya thupi. Kumatithandizanso kuti tizigona tulo tabwino.

“Kupatsa kumatichititsa kukhala osangalala kwambiri kuposa kulandira.”—Machitidwe 20:35.

Tikamapatsa anthu ena ndalama kapena zinthu zina, zimakhala zosavuta kuti tidzalandire thandizo tikadzafunikira. Howard, yemwe amakhala ku England, anati: “Tikamayesetsa kukhala opatsa komanso kuthandiza ena, ine ndi mkazi wanga sitiona kuti tikuvutitsa anthu ikafika nthawi yoti nawonso atithandize.” N’zoona kuti anthu amene amapereka zinthu kuchokera mumtima, sayembekezera kuti anthu adzawabwezere. Koma kupatsa kumawathandiza kuti apeze anzawo apamtima omwe angawathandize akavutika.

“Khalani opatsa ndipo inunso anthu adzakupatsani.”—Luka 6:38.

ZIMENE MUNGACHITE

Muzigawira ena zomwe muli nazo. Ngakhale mutakhala kuti mulibe zinthu zambiri, mukhoza kukhala ndi kenakake komwe mungagawire anthu ena. Mwachitsanzo, mukhoza kuwaitana kuti adzadye chakudya. Duncan ndi banja lake, omwe amakhala ku Uganda, ndi osauka koma ali ndi mtima wopatsa. Duncan anati: “Lamlungu, ine ndi mkazi wanga timakonda kuitana munthu kunyumba n’kudya naye chakudya chosafuna zambiri. Timasangalala kucheza ndi anthu.”

Komabe tiyenera kukhala osamala pa nkhani yopatsayi. Si bwino kumangopereka zinthu kwa ena mpaka banja lanu kumavutika.—Yobu 17:5.

Tayesani izi: Itanani munthu wina kunyumba kwanu kuti mudzadye naye chakudya chosafuna zambiri kapena kumwa naye zakumwa. Ngati muli ndi zinthu zomwe simuzigwiritsa ntchito, mukhoza kupatsa anzanu kapena maneba omwe angazigwiritse ntchito.


Mukhoza kukhala wopatsa m’njira zinanso. Mphatso zina zabwino kwambiri sitichita kugula. Mwachitsanzo, tingapatule nthawi yathu kuti tichite zinthu zina zothandiza anthu ena. Mawu abwino akhozanso kukhala mphatso. Choncho muziyamikira anthu ena komanso kuwauza kuti mumawakonda.

Tayesani izi: Thandizani anthu ena ntchito zapakhomo, kukonza zomwe zawonongeka kapena kukawagulira zinthu. Lembani khadi kapena meseji kwa mnzanu, ngakhale yongomuuza kuti mukumuganizira.

Mukakhala wopatsa, mumadalitsidwa kwambiri.

“Musaiwale kuchita zabwino ndi kugawira ena zomwe muli nazo.”—Aheberi 13:16.

Banja lina likuthandiza mayi wachikulire kuyeretsa panja pa nyumba yake. Mayiyo akuwapatsa zakumwa.
Trey.

“Ngakhale kuti nyumba yathu ndi yaing’ono, timakonda kuphika chakudya n’kuitana anthu kuti tidzadyere limodzi. Timasangalala kwambiri tikathandiza anzathu. Nthawi zina timawapatsa ndalama koma nthawi zambiri timangowapatsa nthawi yathu. Takhala tikuona umboni wakuti kupatsa kumatichititsa kukhala osangalala kwambiri kuposa kulandira.”—Trey, Israel.

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena