Phunziro 20
Uphungu Umalimbikitsa
1, 2. N’chifukwa chiyani timafunikira uphungu, ndipo timaulandira m’njira yotani?
1 Alambiri a Mulungu woona, nthaŵi zonse ndipo mosakayika konse, amafuna chitsogozo kwa iye m’njira zawo zonse. Mmodzi wa olemba masalmo a Baibulo analemba mwachidaliro kuti: “Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu.” (Sal. 73:24) Ndipo m’pemphero lake lochokera pansi pa mtima Yeremiya anati: “Palibe chokulakani Inu; . . . dzina lake ndi Mulungu wamkulu, wamphamvu, Yehova wa makamu; wamkulu mu upo [“uphungu,” NW], wamphamvu m’ntchito.”—Yer. 32:17-19.
2 Uphungu wa Yehova umadza kwa alambiri ake achikristu lerolino kupyolera m’Mawu ake olembedwa komanso kupyolera m’gulu la atumiki ake enieni. Choncho awo amene alembetsa m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase amazindikira mwamsanga kuti uphungu umene amalandirawo, komanso mmene aphunguwo amauperekera, amatsatiradi chiphunzitso chabwino cha m’Baibulo.
3-5. Fotokozani mmene silipi la Uphungu wa Kulankhula ndi nkhani za m’Maphunziro 21 mpaka 37 zakonzedwera kuti zigwiritsidwe ntchito limodzi.
3 Uphungu wopita patsogolo. Pofuna kuthandiza ophunzira komanso woyang’anira sukulu, pali silipi la Uphungu wa Kulankhula limene laperekedwa. Pasilipi limenelo andandalikapo mfundo zokwanira 36 zoti zithandize ophunzira pokulitsa luso lofotokoza choonadi mogwira mtima. Mfundo iliyonse yalongosoledwa momvekera bwino m’Maphunziro 21 mpaka 37 a buku lino, ndipo phunziro lililonse alisonyeza ndi nambala pasilipi la Uphungu wa Kulankhula. Maphunziro ameneŵa ndi oti agwiritsidwe ntchito limodzi ndi silipi la uphungu. Mudzaona kuti kaŵirikaŵiri maluso aŵiri kapena atatu ogwirizana kwambiri akalankhulidwe aphatikizidwa m’Phunziro limodzi. Izi zakhala choncho chifukwa taona kuti ndi bwino kuwapenda nthaŵi imodzi.
4 Kudzakhala kowapindulitsa aja olembetsa chatsopano m’sukulu kumakonzekera bwino lomwe, akumaganiza mfundo zondandalikidwa pasilipi la Uphungu wa Kulankhula. Pankhani yawo yoyamba m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase, woyang’anira sukulu (kapena phungu wina ngati olembetsa ndi ochuluka) adzangoyamikira wophunzirayo pamfundo zimene wachitapo bwino. Kenako, phunguyo asumike maganizo pamfundo yofunikira kwambiri chisamaliro kuti wophunzirayo awongolere kalankhulidwe kake, ndipo agaŵire wophunzirayo mfundo yoti akagwirirepo ntchito pankhani yake yotsatira. Ngati wophunzira aliyense afika poti wakhoza bwino pamfundo inayake, phungu ayenera kum’dziŵitsa kuti tsopano apite pamfundo ina pasilipi la uphungu.
5 Ena ophunzira kulankhula nkhani angapite patsogolo mofulumirirapo kwambiri, pamene ena angafunikire kulimbikira pamfundo imodzi yokha panthaŵi imodzi m’malo moyesa kukwaniritsa mfundo zonse zofotokozedwa m’Phunziro lonse. Ndipo ophunzira ena angalangizidwe kulankhula nkhani zingapo pamene akugwirira ntchito pamfundo imodzi yovuta, kotero kuti alidziŵe bwino kwambiri luso lakulankhula limenelo asanapite ku lina.
6, 7. Ndi mfundo zotani zimene woyang’anira sukulu ayenera kuperekapo uphungu?
6 Uphungu wopatsidwa kwa wophunzira aliyense atatha nkhani yake uyenera kuperekedwa mokoma mtima, ndi cholinga chothandiza wophunzirayo kuti apite patsogolo powongolera luso lake lakulankhula. Komabe, uphungu uliwonse wopatsidwa kwa wopereka nkhani yolangiza kapena mfundo zazikulu za m’Baibulo, uyenera kuperekedwa m’seri sukulu itatha. Mlankhuli ameneyu ayenera kupatsidwa uphungu makamaka ngati wadya nthaŵi yosonyezedwayo. Wolankhula nkhani yolangiza ayenera kuyesetsa kupereka nkhani yachitsanzo m’mbali zonse, ndipo akatero uphungu wam’seri ungakhale wosafunikira.
7 Nthaŵi zonse uphungu uyenera kuperekedwa pamfundo zimene wophunzirayo analangizidwa kuti agwirirepo ntchito. Komabe, ngati pali mbali ina pankhaniyo imene iye wachita bwino kwambiri, phunguyo angaiphatikize pakuyamikira kwake, koma mfundo imeneyo asaichonge pasilipi la uphungu. Zizindikiro zogwiritsa ntchito ndi izi: “L” (Limbikirani chimenechi) ngati wophunzirayo afunikirabe kuyesetsa kuwongolera luso limenelo la kulankhula; “W” (Wawongolera) ngati wophunzira anayesapo kale kukonza luso limenelo ndipo akuonetsa kuti wawongolera koma ulendo wina angachite bwino koposa; “B” (Bwino) ngati luso limene akugwirirapo ntchito walisonyeza bwino moti afunikira kupita pamfundo ina pokonzekera nkhani yotsatira m’sukuluyo. Ngati wophunzira ali ndi nkhani yoŵerenga, phungu adzapereka uphungu woyenerana ndi nkhani yamtundu umenewo.
8-10. Pochonga silipi la uphungu, kodi woyang’anira sukulu ayenera kukumbukira chiyani pofuna kulimbikitsa ena kupita patsogolo?
8 M’pofunika kuti woyang’anira sukulu azikhala wosamala kwambiri kuti apindulitse onse ndi uphungu wake. Ngati wolankhula nkhani ali watsopano kwambiri, chofunika kwambiri ndicho kungom’limbikitsa. Komanso alipo ophunzira ena amene akhala kanthaŵi ndithu m’sukulu, oti ali ndi khama lokonzekera nkhani zawo, nayesa kusamalira maluso a kulankhula amene amagaŵiridwa kugwirirapo ntchito, koma luso lawo n’kukhalabe lochepa. M’zochitika zoterozo, ngati iwo aonetsa luso lina ngakhale pamlingo wochepa chabe, woyang’anira sukulu angalembe “B” pasilipi la uphungu ndi kulola wophunzirayo kupita pamfundo ina.
9 Komanso, mlankhuli wina angakhale ndi chidziŵitso chochulukirapo kapena luso lachibadwa lokulirapo, koma, mwina chifukwa chotanganidwa ndi ntchito zina, sanapatule nthaŵi yoti aŵerenge za maluso akulankhula amene anagaŵiridwa kwa iye, ndiye n’kulephera kulankhula bwino nkhani yake. Zikakhala choncho, kungakhale kulepheretsa wophunzirayo kupita patsogolo ngati woyang’anira sukulu alemba “B” pasilipi la uphungu namuuza kupita pamfundo ina. Ngati nkhaniyo inali yamtundu woti mfundo yogaŵiridwayo ikanasonyezedwa, phunguyo alembe “L” (Limbikirani chimenechi) ndi kupereka chithandizo mokoma mtima kwa wophunzirayo kuti apite patsogolo. Mwa njira imeneyi ophunzira adzalimbikitsidwa kuona nkhani iliyonse kukhala chizindikiro chosonyeza kupita kwawo patsogolo, osati chabe kukwaniritsa gawo lawo.
10 Kumbukirani kuti kuphunzira kalankhulidwe ka nkhani kumeneku n’kwapang’onopang’ono. Musayembekeze kukhala mlankhuli wokhoza bwino nthaŵi yomweyo. Zimachitika pang’onopang’ono, koma wina akhoza kuchita mofulumirirapo ngati aikirapo khama kwambiri. Ngati mudzasinkhasinkha panjira zosiyanasiyana zoperekedwa m’pologalamu imeneyi yophunzitsa kalankhulidwe ndi kuchita khama kumakonzekera nkhani zanu, kupita patsogolo kwanu kudzaonekera kwa onse.—1 Tim. 4:15.
11-16. Ndi malangizo otani amene phungu amatsatira pofuna kulimbikitsa ena ndi uphungu wake?
11 Phungu. Woyang’anira sukulu ayenera kupenda mosamala nkhani za mlungu uliwonse kotero kuti adziŵe ngati nkhaniyo yalankhulidwa bwino ndi kuti akhoze kuwongolera zolakwa zilizonse. Komabe, sayenera kufika pamlingo woti sakondweranso ndi nkhanizo chifukwa chokhala wosuliza kwambiri za mmene nkhani zikulankhulidwira. Iyenso ayenera kupindula ndi choonadi chabwino chomwe chikulongosoledwa.
12 Popereka uphungu nthaŵi zonse ayenera kuyamba ndi mawu oyamikira khama la wophunzira. Ndiyeno apitirize kukambapo pamfundo za pasilipi la uphungu zimene mlankhuliyo akugwirirapo ntchito. Ngati mfundo ina ikufunikirabe kuwongolera, si bwino kugogomeza mmene mlankhuliyo walepherera, koma mmene angawongolere mfundoyo. Akatero uphunguwo udzalimbikitsa mlankhuliyo komanso ena omvetsera.
13 Sikokwanira kungouza mlankhuli kuti wachita bwino kapena kuti afunikira kulimbikirabe paluso lakutilakuti la kulankhula. Kudzakhala kothandiza wina aliyense amene alipo ngati phunguyo afotokoza chifukwa chake nkhaniyo inali bwino kapena chifukwa chake pakufunikira kuwongolera komanso mmene kuwongolerako angakuchitire. Ndiponso, kudzakhala kopindulitsa ngati iye asonyeza mmene luso la kulankhula limene akufotokozalo liliri lofunika kaamba ka utumiki wakumunda kapena pamisonkhano yampingo. Mwa kutero, adzathandiza mpingo wonse kuzindikira mfundo imeneyo ndipo adzalimbikitsanso wophunzirayo kupitirizabe kuisamalira.
14 Si udindo wake phunguyo kubwereramo m’nkhani ya wophunzira. Iye ayenera kuchita mwachidule ndipo molunjika pamfundo ya uphungu wake, akumasamala kuthera mphindi ziŵiri zokha pankhani iliyonse ya wophunzira. Mwa kutero, uphunguwo ndi maganizo operekedwawo sadzaphimbika ndi mawu ambirimbiri. Ndiponso, m’pofunika kutchulira wophunzirayo masamba pamene angapeze chidziŵitso chochulukirapo pamfundo imene mwafotokoza.
15 Zolakwa zazing’ono monga katchulidwe ka mawu kapena galamala si zinthu zazikulu zoti n’kuziyang’anira. M’malo mwake, phungu ayenera kusamala za mmene kalankhulidwe ka wolankhulayo kakukhudzira anthu. Kodi nkhaniyo n’njopindulitsa ndi yopatsa chidziŵitso? Kodi n’njolinganizika bwino komanso yosavuta kutsatira? Kodi ikulankhulidwa moona mtima, mosamala, ndi mokhutiritsa? Kodi nkhope yake ndi manja ake polankhula zikusonyeza kuti akukhulupirira zimene akunenazo ndi kuti akufunitsitsa kuti omvetserawo amve choonadi chabwino m’malo mokopeka ndi kalankhulidwe kake? Ngati mbali zofunika zimenezi zasamalidwa bwino, omvetsera sadzaona n’komwe zolakwa za apa ndi apo m’katchulidwe ka mawu kapena m’galamala.
16 Uphungu woperekedwa m’sukulu yateokalase nthaŵi zonse uyenera kuperekedwa m’njira yokoma mtima ndi yothandiza. Cholinga chachikulu chiyenera kukhala chothandiza wophunzirayo. Ganizirani za umunthu wa amene mukufuna kum’patsa uphunguyo. Kodi n’ngwa mtima wapachala? Kodi sanaphunzire kwenikweni kusukulu? Kodi pali zifukwa zololera zolakwa zake? Uphungu uyenera kupangitsa woulandirayo kuona kuti akuthandizidwa, osati kusulizidwa. Tsimikizani kuti akuumvetsa uphunguwo ndipo akuuona kukhala woyenera.
17-19. Kuti apange kuwongolera kwakukulu pankhani iliyonse, kodi wophunzira ayenera kuchitanji asanakonze nkhani iliyonse ndi pambuyo poilankhula?
17 Kupindula ndi uphungu. Mukapatsidwa nkhani m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase kumbukirani kuti cholinga chanu chokalankhulira nkhaniyo sindicho kungolongosolera mpingo mfundo zolangiza, komanso kuwongolera luso lanu la kalankhulidwe. Kuti mukhale wokhoza m’mbali imeneyi, m’pofunika kupatula nthaŵi yopenda maluso a kulankhula amene mwapatsidwa kuti mugwirirepo ntchito. Ŵerengani mosamalitsa Phunziro lonselo m’buku lino pamene akulongosola mfundo imeneyo, kuti mudziŵe mmene iyenera kukhudzira kukonzekera kwanu ndi mmene mungasonyezere luso la kulankhulalo polankhula nkhani yanu. Pofuna kukuthandizani, mbali zazikuluzo za luso lililonse la kulankhula zalembedwa m’zilembo zazikulu zakuda m’buku lino. Zimenezi ndizo mbali zazikulu zoti muzisamalire.
18 Mutalankhula nkhani yanu, mvetserani mosamala uphungu wa pakamwa umene ukuperekedwa. Ulandireni moyamikira. Ndiyeno gwirirani ntchito pambali zofunikira kuwongolera. Ngati mukufuna kufulumiza kupita kwanu patsogolo, musayembekeze kufikira mutapatsidwa nkhani ina. Ŵerengani m’buku lino mbali zimene zikufotokoza mfundo zimene mukufunikira kugwirirapo ntchito. Yesetsani kugwiritsa ntchito maganizo operekedwawo m’kulankhula kwanu kwa tsiku ndi tsiku. Ndipo pofika nthaŵi yoti mulankhule nkhani yanu yotsatira ya wophunzira mungakhale mutazidziŵa bwino.
19 Wophunzira aliyense cholinga chake chiyenera kukhala kuwongokera pankhani iliyonse imene apereka m’sukulu. N’zoona kuti zimenezo zidzafuna khama losalekeza, koma mosapeneka konse, zotsatirapo zake ndi dalitso la Yehova. Kwa aja amene angapeze phindu lalikulu m’maphunziro a Sukulu ya Utumiki Wateokalase, mawu a pa Miyambo 19:20 amakhala ndi tanthauzo lalikulu kwa iwo: “Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimariziro chako.”
[Tchati pamasamba 104, 105]
UPHUNGU WA KULANKHULA
Mlankhuli ․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․
(Dzina Lonse)
Zizindikiro: L - Limbikirani chimenechi
W - Wawongolera
B - Bwino
Deti Na. ya
Nkhani
Mfundo zopatsa chidziŵitso (21)*
Kumveka bwino (21)
Mawu oyamba odzutsa chidwi (22)
Mawu oyamba oyenerana ndi mutu wa nkhani (22)
Mawu oyamba autali woyenera (22)
Mphamvu ya mawu (23)
Kupuma (23)
Kulimbikitsa omvetsera kuŵerenga Baibulo (24)
Kutulutsa malemba koyenera (24)
Kuŵerenga malemba ndi chigogomezo (25)
Kumveketsa bwino tanthauzo la malemba (25)
Kubwereza kogogomeza (26)
Manja (26)
Kugogomeza mutu wa nkhani (27)
Kupangitsa mfundo zazikulu kuonekera (27)
Kuyendera limodzi ndi omvetsera, ntchito ya notsi (28)
Ntchito ya autilaini (28)
Mawu:․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․
․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․
․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․․
* Nambala iliyonse m’mabulaketi ikusonyeza Phunziro la mu Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase mmene luso la kulankhulalo lafotokozedwa.
S-48-CN 3/85 J.G.
Deti Na. ya
Nkhani
Kusadodoma (29)
Mkhalidwe wokambirana (29)
Katchulidwe ka mawu (29)
Kugwirizanitsa nkhani ndi mawu olumikizira (30)
Kulankhula kotsatirika ndi kogwirizanika (30)
Kufotokoza kokhutiritsa (31)
Kuthandiza omvetsera kulingalira (31)
Kugogomeza ganizo (32)
Kusinthasintha mawu (32)
Kutengeka mtima (33)
Mzimu waubwenzi ndi wachifundo (33)
Mafanizo oyenerana ndi nkhani (34)
Mafanizo oyenerana ndi omvetsera (34)
Kugwirizanitsa nkhani ndi utumiki wakumunda (35)
Mawu omalizira oyenera, ogwira mtima (36)
Mawu omalizira autali woyenera (36)
Kusunga nthaŵi (36)
Chidaliro ndi kukhazikika maganizo (37)
Maonekedwe a munthu (37)
DZIŴANI IZI: Pankhani iliyonse phungu adzapereka uphungu wachindunji, mosatsatira kwenikweni dongosolo la mfundozo. Koma adzasamala makamaka mbali zimene wophunzirayo afunikira kuwongolera. Malowo osalembedwapo kanthu pafomupo mungawagwiritse ntchito kupatsira uphungu ophunzira pamfundo zimene sizinandandalikidwe, monga kunena zinthu zolondola, kutchula bwino mawu, kaimidwe, kusankha bwino mawu, galamala, zizoloŵezi, kulankhula zoyenerera, luso lophunzitsa, ndi kumveka bwino kwa liwu ngati kukhala kofunikira. Phungu ayenera kulemba mozungulira m’kabokosi ka mfundo yotsatira pamene wophunzira wamaliza kugwirira ntchito pa mfundo ina. Nambala ya mfundo imeneyo iyenera kusonyezedwa pa silipi lotsatira la Nkhani ya m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase (S-89).
Tchati pamasamba 106, 107
KUFOTOKOZA MWACHIDULE MALUSO A KULANKHULA
Mfundo zopatsa chidziŵitso (21)
Mfundo zolunjika
Zopatsa chidziŵitso omvetsera
Mfundo zothandiza
Kunena mawu olondola
Mfundo zowonjezera zothandiza kumveketsa bwino nkhani
Kumveka bwino (21)
Kufotokoza kosavuta kumva
Kufotokoza mawu osazoloŵereka
Kusachulukitsa mfundo
Mawu oyamba odzutsa chidwi (22)
Mawu oyamba oyenerana ndi mutu wa nkhani (22)
Mawu oyamba autali woyenera (22)
Mphamvu ya mawu (23)
Mphamvu ya mawu pamlingo woyenera
Mphamvu ya mawu yoyenerana ndi mikhalidwe
Mphamvu ya mawu yoyenerana ndi nkhani
Kupuma (23)
Kupuma pachizindikiro chopumira
Kupuma posintha ganizo
Kupuma kogogomeza
Kupuma pamene mkhalidwe wafuna kuti mutero
Kulimbikitsa omvetsera kuŵerenga Baibulo (24)
Mwa Kungotchula lemba
Mwa kulola nthaŵi kuti apeze lemba
Kutulutsa malemba koyenera (24)
Kudzutsa chidwi pa malemba
Kutchula chifukwa choŵerengera lemba
Kuŵerenga malemba ndi chigogomezo (25)
Kugogomeza mawu oyenera
Kugogomeza mwa njira yogwira mtima
Malemba oŵerengedwa ndi mwininyumba
Kumveketsa bwino tanthauzo la malemba (25)
Kulekanitsa mawu ofunika kuwatanthauzira
Mfundo ya mawu oyamba poŵerenga lemba imveketsedwa
Kubwereza kogogomeza (26)
Kubwereza mfundo zazikulu
Kubwereza mfundo zimene sizinamveke
Manja (26)
Manja ofotokoza
Manja ogogomeza
Kugogomeza mutu wa nkhani (27)
Mutu wa nkhani woyenerera
Kubwereza mawu kapena ganizo la mutu wankhani
Kupangitsa mfundo zazikulu kuonekera (27)
Kusachulukitsa mfundo zazikulu
Kufotokoza mfundo zazikulu payokhapayokha
Mfundo zazing’ono ziloza ku mfundo zazikulu
Kuyendera limodzi ndi omvetsera, ntchito ya notsi (28)
Kuyendera limodzi ndi omvetsera mwa kuwayang’ana
Kuyendera limodzi ndi omvetsera mwa mawu owaphatikizamo
Ntchito ya autilaini (28)
Kusadodoma (29)
Mkhalidwe wokambirana (29)
Kugwiritsa ntchito mawu okambirana
Kulankhula nkhani m’njira yokambirana
Katchulidwe ka mawu (29)
Kugwirizanitsa nkhani ndi mawu olumikizira (30)
Ntchito ya mawu olumikizira
Kugwirizanika koyenerana ndi omvetsera anu
Kulankhula kotsatirika ndi kogwirizanika (30)
Mfundo zosanjidwa m’dongosolo labwino
Kugwiritsa ntchito mfundo zoyenerera zokhazokha
Kusasiya mfundo zazikulu
Kufotokoza kokhutiritsa (31)
Kukhazikitsa maziko
Kupereka umboni womveka
Kulongosola kwachidule kogwira mtima
Kuthandiza omvetsera kulingalira (31)
Kusataya mfundo yogwirizanapo
Kufotokoza mfundo momveka bwino
Kuonetsa omvetsera mmene nkhaniyo ikuwakhudzira
Kugogomeza ganizo (32)
Kugogomeza mawu opereka ganizo m’sentensi
Kugogomeza mfundo zazikulu m’nkhani
Kusinthasintha mawu (32)
Kusinthasintha mphamvu ya mawu
Kusinthasintha liŵiro polankhula
Kusinthasintha ukulu wa mawu
Kusinthasintha mawu koyenerana ndi ganizo kapena mzimu wake
Kutengeka mtima (33)
Kuonetsa kutengeka mtima mwa kalankhulidwe kaumoyo
Kutengeka mtima koyenerana ndi nkhani
Mzimu waubwenzi ndi wachifundo (33)
Mzimu waubwenzi uonekera pankhope
Mzimu waubwenzi ndi wachifundo zionekera m’kamvekedwe ka mawu
Mzimu waubwenzi ndi wachifundo woyenerana ndi nkhani
Mafanizo oyenerana ndi nkhani (34)
Osavuta
Kumveketsa bwino tanthauzo lake
Kugogomeza mfundo zofunika kwambiri
Mafanizo oyenerana ndi omvetsera (34)
Onena za zinthu zodziŵika bwino
Abwino
Kugwirizanitsa nkhani ndi utumiki wakumunda (35)
Kumveketsa mawu kwa anthu
Kusankha mfundo zoyenerera
Kuunika phindu la mfundo zoperekedwa
Mawu omalizira oyenera, ogwira mtima (36)
Mawu omalizira ogwirizana mwachindunji ndi mutu wa nkhani
Mawu omalizira osonyeza omvetsera chochita
Mawu omalizira autali woyenera (36)
Kusunga nthaŵi (36)
Chidaliro ndi kukhazikika maganizo (37)
Kukhazikika maganizo kuonekera m’kaimidwe ka munthu
Kukhazikika maganizo kuonekera mwa kulamulira mawu
Maonekedwe a munthu (37)
Kuvalidwe ndi kapesedwe kabwino
Kaimidwe koyenera
Zipangizo zosamalika bwino
Musasonyeze nkhope yosemphana ndi nkhani