Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 5
  • Moyo Wobvuta Uyamba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Moyo Wobvuta Uyamba
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Chifukwa Chake Anataya Malo Ao
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Kodi Moyo Unali Wotani m’Paradaiso?
    Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Adamu ndi Hava Sanamvere Mulungu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Pali Wina Wokulirapo
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 5

NKHANI 5

Moyo Wobvuta Uyamba

KUNJA kwa munda wa Edene, Adamu ndi Hava anali ndi mabvuto ambiri. Anayenera kugwira ntchito zolimba kuti apeze chakudya. M’malo mwa mitengo ya zipatso yokongola, anaona minga ndi mitula zikumera ponse-ponse. N’zimene zinachitika pamene Adamu ndi Hava sanamvere Mulungu ndipo sanakhale’nso mabwenzi Ake.

Koma choipa kwambiri, iwo anayamba kufa. Pajatu, Mulungu anawachenjeza kuti akafa ngati akadya zipatso za mtengo wina. Tsiku lomwe anadya anayamba kufa. Kunali kopusa chotani kwa iwo kuti sanamvere Mulungu!

Ana ao onse anabadwa Mulungu atawathamangitsa m’munda wa Edene. Zikutanthauza kuti ana’wo nawo’nso akalamba ndi kufa.

Adamu ndi Hava akanamvera Yehova, moyo ukanakhala wachimwemwe kwa iwo ndi ana ao. Iwo akanakhala ndi moyo kosatha m’chimwemwe pa dziko lapansi. Palibe akanakalamba, kudwala ndi kufa.

Mulungu amafuna kuti anthu akhale ndi moyo kosatha m’chimwemwe, ndipo akulonjeza kuti tsiku lina adzatero. Dziko lonse silidzangokongola kokha, koma anthu onse adzakhala athanzi. Ali yense pa dziko adzakhala bwenzi labwino kwa ali yense ndi Mulungu.

Koma Hava sanali’nso bwenzi la Mulungu. Tsono pobala ana ake, sikunali kosam’bvuta. Anamva ululu. Kusamvera Yehova kunam’dzitsera’di chisono chochuluka, kodi si choncho?

Adamu ndi Hava anali ndi ana amuna ndi akazi ambiri. Atabadwa mwana wao wamwamuna woyamba, anam’cha Kaini. Wachiwiri anam’cha Abele. Kodi n’chiani chimene chinawachitikira? Kodi mukudziwa?

Genesis 3:16-23; 4:1, 2; Chivumbulutso 21:3, 4.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena