Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 31
  • Mose ndi Aroni Aona Farao

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mose ndi Aroni Aona Farao
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Miliri Itatu Yoyambirira
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mose ndi Aroni—Alengezi Olimba Mtima a Mawu a Mulungu
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Miliri Inanso 6
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Yehova Ndani?
    Nsanja ya Olonda—1993
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 31

NKHANI 31

Mose ndi Aroni Aona Farao

MOSE atabwerera ku Igupto, anauza mkulu wake Aroni zonse ponena za zozizwitsa’zo. Ndipo Mose ndi Aroni atazisonyeza kwa Aisrayeli, anthu onse akukhulupirira kuti Yehova anali nawo.

Ndiyeno Mose ndi Aroni anamka kukaonana ndi Farao. Iwo anamuuza kuti: ‘Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, “Lola anthu anga apite kwa masiku atatu, kuti akandilambire m’chipululu.” Farao anayankha nati: ‘Sindikhulupirira Yehova. Ndipo sindidzalola Israyeli apite.’

Farao anakwiya, chifukwa anthu’wo anafuna nthawi ya kusakhala pa ntchito kuti akalambire Yehova. Chotero anawaumiriza kugwira ntchito mwamphamvu koposa kale. Aisrayeli anasuliza Mose pa kuchitiridwa kwao moipa, ndipo Mose anamva chisoni. Koma Yehova anamuuza kusadera nkhawa. ‘Ndidzam’chititsa kuwalola kupita,’ anatero Yehova.

Mose ndi Aroni anakaona’nso Farao. Nthawi ino iwo akuchita chozizwitsa. Aroni anaponya pansi ndodo yake, nikhala chinjoka. Koma amatsenga a Farao nawo’nso anaponya zao, nazionekera njoka. Koma, onani! Njoka ya Aroni ikumeza njoka za amatsenga’wo. Farao sakulolabe Aisrayeli kumuka.

Nthawi inafika kenako yoti Yehova aphunzitse Farao phunziro. Kodi mukudziwa m’mene anachitira? Kunali mwa kudzetsa miriri 10, kapena zobvuta zazikulu, pa Igupto.

Miriri yambiri itachitidwa, Farao akuitana Mose, nati: ‘Letsa mliri’wo, ndipo ndidzawalola amuke.’ Koma utaleka mliri’wo, Farao ankasintha maganizo ake. Sankalola anthu’wo kumuka. Koma, kenako, utatha mliri wa 10, Farao akulola Aisrayeli kumuka.

Kodi mukudziwa uli wonse wa miriri 10’yo? Tsegulani kutseri ndipo tiyeni tiphunzire za iyo.

Eksodo 4:27-31; 5:1-23; 6:1-13, 26-30; 7:1-13.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena