Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 85
  • Yesu Abadwira m’khola

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Abadwira m’khola
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • “Uyu Ndiye Mwana Wanga”
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
  • “Uyu Ndiye Mwana Wanga”
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • Kodi Yesu Anabadwa Liti Ndipo Anabadwira Kuti?
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Angelo Analengeza za Kubadwa kwa Yesu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 85

NKHANI 85

Yesu Abadwira m’khola

KODI mukudziwa kakhanda’ka? Inde, ndiko Yesu. Wangobadwa kumene m’khola. Khola ndiro kumene zifuyo zimasungidwa. Mariya wagoneka Yesu modyera ng’ombe, amene ali malo m’mene mumasungidwira zakudya za aburu ndi zifuyo zina. Koma kodi n’chifukwa ninji iye ndi Yosefe ali muno limodzi ndi zinyama’zi? Awa sindiwo malo obadwira mwana kodi si choncho?

Ai, sindiwo. Koma nachi chifukwa chake ali muno: Wolamulira wa Roma, Kaisara Augusto, anapanga lamulo lakuti ali yense ayenera kubwerera ku mzinda umene iye anabadwira kukalembetsa dzina lake m’kaundula. Eya, Yosefe anabadwira muno m’Betelehemu. Koma pofika iye ndi Mariya, panalibe malo pali ponse kaamba ka iwo. Chotero iwo ayenera kudzakhala muno ndi zinyama’zi. Ndipo pa tsiku lomwe’li Mariya akubala Yesu! Koma, monga momwe mukuonera, ali bwino.

Kodi mukuona abusa’wo akudza kudzaona Yesu? Iwo anali kubusa usiku akuyang’anira nkhosa zao, ndipo kuunika kunawawalira. Anali mngelo! Abusa’wo anaopa kwambiri. Koma mngelo’yo anati: ‘Musaope! Ndakutengerani mbiri yabwino. Lero lino, m’Betelehemu, Kristu Ambuye anabadwa. Iye adzapulumutsa anthu! Mudzam’peza atakulungidwa mu msalu atagona modyera ng’ombe.’ Mwadzidzidzi angelo ambiri akudza nayamba kutamanda Mulungu. Chotero pa nthawi yomweyo abusa’wa akufulumira kukaona Yesu, ndipo tsopano am’peza.

Kodi mukudziwa chifukwa chake Yesu ali wapadera kwambiri? Kodi mukudziwa amene iye ali kweni-kweni? Pajatu, m’nkhani yoyambirira ya bukhu’li tinalongosola za Mwana woyamba wa Mulungu. Mwana’yu anagwira ntchito limodzi ndi Yehova m’kulenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi chinthu china chiri chonse. Eya, amene’yu ndiye Yesu’yo!

Inde, Yehova anatenga moyo wa Mwana wake kuuchotsa kumwamba nauika m’mimba mwa Mariya. Pomwepo mwana anayamba kukula m’mimba mwakemo monga momwe’di ana ena amakulira m’mimba mwa amao. Koma mwana uyu anali Mwana wa Mulungu. Potsirizira pake Yesu anabadwa muno m’khola la m’Betelehemu. Kodi mukuona tsopano chifukwa chake angelo’wo anali achimwemwe kwambiri kukhala okhoza kunena zakuti Yesu anali atabadwa?

Luka 2:1-20.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena