Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gt mutu 10
  • Maulendo a ku Yerusalemu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Maulendo a ku Yerusalemu
  • Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Nkhani Yofanana
  • Yosefe ndi Banja Lake Anapita ku Yerusalemu
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Zimene Yesu Anachita Ali Wamng’ono
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mnyamata Yesu m’Kachisi
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Yesu Anaphunzira Kumvera
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
gt mutu 10

Mutu 10

Maulendo a ku Yerusalemu

NGULULU yafika. Ndipo ndinthaŵi yakuti banja la Yosefe, limodzi ndi mabwenzi ndi achibale, apange ulendo wawo wachaka ndi chaka wopita ku Yerusalemu kukasunga Paskha. Pamene akuchoka paulendo umene uli pafupifupi makilomitala 100, pali kuchita chidwi kwa nthaŵi zonse. Tsopano Yesu ali ndi zaka 12 zakubadwa, ndipo akuyang’anira mtsogolo ndi chikondwerero chapadera kuphwandolo.

Kwa Yesu ndi banja lake, Paskha sali chochitika cha tsiku limodzi lokha. Iwo akukhalakonso kwa masiku asanu ndi aŵiri otsatira, kaamba ka Phwando la Mkate Wopanda Chotupitsa, limene akulingalira kukhala mbali ya nyengo ya Paskha. Monga chotulukapo, ulendo wonse wochokera kwawo ku Nazarete, kuphatikizapo kukakhala m’Yerusalemu umatenga pafupifupi masabata aŵiri. Koma chaka chino, chifukwa cha kanthu kena kamene kakuphatikizapo Yesu, ukutenga nthaŵi yotalikirapo.

Vutolo likudziŵika paulendo wobwerera kuchokera ku Yerusalemu. Yosefe ndi Mariya akulingalira kuti Yesu ali m’kagulu ka achibale ndi mabwenzi amene akuyenda nawo. Komabe iye sakuwoneka pamene akuima usiku, ndipo iwo akumfunafuna pakati pa atsamwali awo oyenda nawo. Iye sakupezeka kulikonse. Chotero Yosefe ndi Mariya akubwereranso ku Yerusalemu kukamfunafuna.

Kwa tsiku lathunthu iwo akumfunafuna, koma mosaphula kanthu. Tsiku lachiŵiri iwo sakumpezanso. Potsirizira, patsiku lachitatu, iwo akupita kukachisi. Kumeneko m’chimodzi cha zipinda zake, iwo akuwona Yesu atakhala pakati pa aphunzitsi Achiyuda, akumawamvetsera nawafunsa mafunso.

“Mwanawe, wachitiranji ife chotero?” Mariya akufunsa motero. “Tawona atate wako ndi ine tinali kufunafuna iwe ndi kuda nkhaŵa.”

Yesu akudabwa kuti iwo sanadziŵe kumene angampeze. ‘Kodi nchifukwa ninji munakandifunafuna?’ iye akufunsa motero. ‘Kodi simunadziŵe kuti ine ndiyenera kukhala m’nyumba ya Atate wanga?’

Yesu sangathe kumvetsetsa chifukwa chimene makolo ake sanadziŵire za ichi. Pamenepo Yesu, akubwerera kunyumba pamodzi ndi makolo ake napitirizabe kuwamvera. Iye akupitirizabe kupita patsogolo m’nzeru ndi m’kusinkhuka ndi kuyanjidwa ndi Mulungu ndi anthu. Inde, kuyambira paubwana wake kumka mtsogolo, Yesu akupereka chitsanzo chabwino kwambiri osati kokha m’kufunafuna zinthu zauzimu komanso m’kusonyeza ulemu kwa makolo ake. Luka 2:40-52; 22:7.

▪ Kodi ndiulendo wa m’ngululu wotani umene Yesu akupanga mokhazikika pamodzi ndi banja lake, ndipo ngwautali motani?

▪ Kodi nchiyani chimene chikuchitika paulendo umene akupanga pamene Yesu ali ndi zaka 12 zakubadwa?

▪ Kodi ndichitsanzo chotani chimene Yesu akupereka kwa achichepere lerolino?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena