Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 14-15
  • ‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Aisrayeli ndi Mitundu Yowazungulira
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Yesu “m’Dziko la Ayuda”
    ‘Onani Dziko Lokoma’
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 14-15

‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’

Mafuko ndi Oweruza

SIMUNGAVUTIKE kupeza Phiri la Tabori (F4) pa mapuŵa. Phiri limeneli lili kum’mwera chakumadzulo kwa Nyanja ya Galileya, m’Chigwa cha Yezreeli. Tayerekezerani kuti mukuona asilikali 10,000 atasonkhana pamwamba pa phirili. Yehova anagwiritsa ntchito Woweruza Baraki ndi mneneri wamkazi Debora kusonkhanitsa Israyeli kuti alimbane ndi Mfumu Yabini ya Akanani yomwe inakhala ikuwapondereza kwa zaka 20. Motsogoleredwa ndi Sisera, mkulu wa asilikali, magaleta 900 a Yabini, okhala ndi zikwakwa zachitsulo zoopsa kwambiri anachoka nawo ku Haroseti kubwera khwawa la Kisoni, pakati pa Megido ndi Phiri la Tabori.

Woweruza Baraki anatsogolera amuna a Israyeli kupita kuchigwako kukamenya nkhondo ndi asilikali a Sisera. Yehova anawathandiza kupambana nkhondoyo mwa kuchititsa kuti deralo lisefukire madzi zomwe zinatitimitsa magaleta a Sisera, Akananiwo n’kusoŵa pogwira. (Ower. 4:1–5:31) Aka kanali kamodzi chabe mwa maulendo ambirimbiri omwe Israyeli anapambana nkhondo mothandizidwa ndi Mulungu m’nthaŵi za Oweruza.

Kanani atalandidwa, dzikoli linagaŵidwa kwa mafuko a Israyeli. Onani malo amene mafuko osiyanasiyana amene sanali Alevi anakhala. Fuko laling’ono la Simeoni linapatsidwa midzi m’dera la Yuda. Yoswa atamwalira, moyo wauzimu ndiponso makhalidwe a mtunduwu zinasokonezeka kwambiri. Israyeli ‘anasautsika kwambiri’ ndi adani. Powachitira chifundo, “Yehova anautsa oweruza,”—amuna 12 okhulupirika ndi olimba mtima—omwe anapulumutsa Israyeli pazaka 300.—Ower. 2:15, 16, 19.

Woweruza Gideoni anagwiritsa ntchito asilikali 300 okha, opandanso zida zokwanira koma amphamvu, kugonjetsa asilikali 135,000 a Amidyani. Nkhondoyi anamenyera pakati pa mapiri a Giliboa ndi More. Atawagonjetsa adaniwo pakumenyanako, Gideoni anawathamangitsira kum’maŵa, mpaka m’chipululu.—Ower. 6:1–8:32.

Yefita, Mgileadi wa fuko la Manase, anapulumutsa midzi ya Aisrayeli ya kum’maŵa kwa Yordano kwa Aamoni omwe ankaipondereza. Kuti apambane, mwachionekere Yefita anadutsa Msewu Wachifumu womwe unkadutsa ku Ramoti Gileadi mpaka kudera la Aroeri.—Ower. 11:1–12:7.

Kudera lakugombe lozungulira Gaza ndi Asikeloni ndi komwe Samsoni anazunzira Afilisti. Gaza ali m’dera la madzi ambiri lotchuka ndi ulimi. Samsoni anagwiritsa ntchito nkhandwe 300 potentha minda ya Afilisti ya tirigu, ya mphesa, ndiponso ya azitona.—Ower. 15:4, 5.

Malinga ndi nkhani za m’Baibulo kapena mafuko awo, oweruzaŵa anali m’Dziko Lolonjezedwa lonselo. Zilibe kanthu kuti woweruza anagwirira kuti ntchito yake, koma Yehova anali kuwasamalira bwinobwino anthu ake olapa panthaŵi ya mavuto.

[Mapu patsamba 15]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Mafuko ndi Oweruza

Oweruza

1. Otiniyeli (Tribe of Manasseh)

2. Ehudi (Tribe of Judah)

3. Samagara (Tribe of Judah)

4. Baraki (Tribe of Naphtali)

5. Gideoni (Tribe of Issachar)

6. Tola (Tribe of Manasseh)

7. Yairi (Tribe of Manasseh)

8. Yefita (Tribe of Gad)

9. Ibzani (Tribe of Asher)

10. Eloni (Tribe of Zebulun)

11. Abidoni (Tribe of Ephraim)

12. Samsoni (Tribe of Judah)

Malire a Mafuko (Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Midzi ya Manase ya M’dera la Fuko Lina

E4 Doro

E5 Megido

E5 Taanaki

F4 Eni-doro

F5 Betiseani (Betisani)

F5 Ibleamu (Gati-rimoni)

Midzi ya Simeoni ya M’dera la Fuko Lina

C9 Saruheni (Saraimu) (Siliimu)

C10 Beti-lebaotu (Betibiri)

D8 Eteri (Tokeni)

D9 Zikilaga

D9 Aini

D9 Hazar-susah?

D9 Asana

D9 Beer-sheba

D10 Hazari-susa?

E9 Etamu

E9 Beti- malikabotu

E9 Betueli? (Kesili?)

E9 Seba? (Yesuwa)

E10 Baalata-beeri (Baala)

E10 Ezemu

Midzi ya Alevi Yopulumukirako

E8 Hebroni

F3 Kedesi

F6 Sekemu

H4 Golani

H5 Ramoti Gileadi

H8 Bezeri

Njira Zazikulu

B10 Via Maris

G10 Msewu Wachifumu

Mafuko a Israyeli

DANI (D7)

D7 Yopa

E8 Zola

YUDA (D9)

C8 Asikeloni

C9 Gaza

C9 Saruheni (Saraimu) (Siliimu)

C10 Beti-lebaotu (Betibiri)

C12 Azimoni

C12 Kadesi

D7 Yabineli

D8 Eteri (Tokeni)

D9 Zikilaga

D9 Aini

D9 Hazari-susa?

D9 Asana

D9 Beer-sheba

D10 Hazari-susa?

E8 Leki

E8 Betelehemu

E8 Hebroni

E9 Etamu

E9 Beti- malikabotu

E9 Betueli? (Kesili?)

E9 Seba? (Kasili)

E10 BBaalata-beeri (Baala)

E10 Ezemu

F8 Yerusalemu

ASERI (E3)

E2 Turo

E4 Haroseti

E4 Dor

F1 Sidoni

MANASE (E5)

E6 Samiri (Samariya)

E6 Piratoni

F6 Sekemu

G5 Abelemehola

EFRAIMU (E7)

E7 Timinati-sera

F6 Tapuwa

F6 Silo

F7 Beteli (Luzi)

NAFITALI (F3)

F2 Beth-anath

F3 Kedesh

G3 Hazor

ZEBULONI (F4)

E4 Betelehemu

ISAKARA (F5)

E5 Megido

E5 Kedesi (Kisioni)

E5 Taanaki

F4 Eni-doro

F5 Betesita

F5 Betiseani (Betisani)

F5 Ibleamu (Gati-rimoni)

BENJAMINI (F7)

F7 Giligala

DANI (G2)

G2 Dani (Laisi)

MANASE (H3)

H4 Golani

GADI (H6)

G6 Sukoti

G6 Penieli

G6 Mizipa (Mizepe)

G7 Yogebeha

H5 Ramoti-Gileadi

H7 Raba

H7 Abelikerami

RUBENI (H8)

G7 Hesiboni

G9 Aroeri

H7 Miniti

H8 Bezeri

[Malo ena]

I1 Damasiko

[Mapiri]

F4 Phiri la Tabori

F4 More

F6 Phiri la Ebala

F5 Phiri la Giliboa

F6 Phiri la Gerizimu

[Nyanja]

C5 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

F9 Nyanja ya Mchere

G4 Nyanja ya Galileya

[Mitsinje]

B11 C. cha Igupto

F6 Mtsinje wa Yordano

G6 C. cha Yaboki

G9 C. cha Arinoni

G11 C. cha Zaredi

[Chithunzi patsamba 14]

Phiri la Tabori, m’dera la Isakara, phiri limeneli lili m’chigwa cha Yezreeli

[Chithunzi patsamba 14]

Kisoni atasefukira anatitimitsa magaleta a Sisera

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena