Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 16-17
  • Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Aisrayeli ndi Mitundu Yowazungulira
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Yesu “m’Dziko la Ayuda”
    ‘Onani Dziko Lokoma’
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 16-17

Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo

MULUNGU analonjeza kuti adzapatsa mbewu ya Abramu dziko lonselo ‘kuyambira pa mtsinje wa Aigupto kufikira . . . mtsinje wa Firate.’ (Gen. 15:18; Eks. 23:31; Deut. 1:7, 8; 11:24) Yoswa ataloŵa m’Kanani, panapita zaka pafupifupi 400 kuti Dziko Lolonjezedwa lifike kumalire amenewo.

Mfumu Davide inagonjetsa ufumu wa Zoba wachiaramiya, umene unafika mpaka ku Firate kumpoto kwa Suriya.a Kum’mwera, dera la Davide linafika kumalire a Igupto chifukwa chogonjetsa Afilisti.—2 Sam. 8:3; 1 Mbiri 18:1-3; 20:4-8; 2 Mbiri 9:26.

Malire a M’Nthawi ya Solomo
Misewu ya M’Nthawi ya Davide ndi Solomo

Kenako, Solomo analamulira “kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti ndi kumalire a Aigupto,” ndipo anachitira chithunzi ulamuliro wamtendere wa Mesiya. (1 Maf. 4:21-25; 8:65; 1 Mbiri 13:5; Sal. 72:8; Zek. 9:10) Ngakhale ndi tero, dera limene Israyeli anakhalamo linkanenedwa kuti linayambira “ku Dani kufikira ku Beereseba.”—2 Sam. 3:10; 2 Mbiri 30:5.

Mfumu Solomo sinamvere Mulungu chifukwa chakuti inadzichulukitsira akavalo ndi magaleta. (Deut. 17:16; 2 Mbiri 9:25) Iye ankatha kuyendetsa zimenezi panjira ndi misewu yosiyanasiyana. (Yos. 2:22; 1 Maf. 11:29; Yes. 7:3; Mat. 8:28) Ndi njira zochepa chabe zimene tikudziŵa kwambiri, monga “msewu wokwera kuchokera ku Beteli kumka ku Sekemu, ndi kum’mwera kwa Lebona.”—Ower. 5:6; 21:19.

Buku lakuti The Roads and Highways of Ancient Israel limanena kuti: “Chinthu chodziŵika chimene chimavutitsa zinthu kwambiri pofufuza za misewu ya m’Israyeli wakale n’chakuti sitingathe kudziŵa bwinobwino mmene misewu ya dzikolo ya nyengo ya m’Chipangano Chakale inali kudutsa popeza misewuyo inafafanizika chifukwa chakuti [nthaŵi imeneyo] misewu inalibe tala.” Komabe, mmene deralo lilili komanso zotsala za midzi yakale imeneyi zomwe zafukulidwa zimasonyeza mmene misewu yambiri inadutsa.

Nthaŵi zambiri misewu inathandiza kwambiri asilikali pa kayendedwe kawo. (1 Sam. 13:17, 18; 2 Maf. 3:5-8) Poukira Israyeli, Afilisti anayenda ulendo kuchoka ku Ekroni ndi Gati mpaka kudera lina “pakati pa Soko ndi Azeka.” Asilikali a Saulo anakumana nawo kumeneko ‘kuchigwa cha Ela.’ Davide atapha Goliati, Afilisti anathaŵa kubwerera ku Gati ndi Ekroni, ndipo Davide anakwera ku Yerusalemu.—1 Sam. 17:1-54.

Midzi ya Lakisi (D10), Azeka (D9), ndi Betesemesi (D9) inali m’njira zachilengedwe zodutsa dera la Shefela kuloŵera ku mapiri a Yuda. Choncho midzi imeneyi inkathandiza kwambiri poletsa adani odutsa panjira ya Via Maris kuti asaloŵe m’kati mwa dera la Israyeli.—1 Sam. 6:9, 12; 2 Maf. 18:13-17.

[Mawu a M’munsi]

a Dera la Rubeni linafika mpaka ku Chipululu cha Suriya, ndipo chipululucho kum’maŵa kwake chinathera mu Firate.—1 Mbiri 5:9, 10.

[Bokosi patsamba 16]

MABUKU A M’BAIBULO OLEMBEDWA NTHAŴIYI:

1 ndi 2 Samueli

Masalmo (mbali yake ina)

Miyambo (mbali yake ina)

Nyimbo ya Solomo

Mlaliki

[Mapu patsamba 17]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Deralo ndi Njira zake Nthaŵi Imene Ufumu Unali Umodzi

Malire a M’nthawi ya Solomo

Tifisa

Hamati

Tadimori

Berotai (Kuni?)

Sidoni

Damasiko

Turo

Dani

Yerusalemu

Gaza

Aroeri

Beereseba

Tamara

Ezioni Geberi

Elati (Eloti)

[Mitsinje]

Firate

C. cha Igupto

Misewu ya M’nthawi ya Davide ndi Solomo

B10 Gaza

C8 Yopa

C9 Asidodo

C10 Asikeloni

C11 Zikilaga

C12 CHIPULULU CHA PARANA

D5 Doro

D6 Heferi

D8 Afeki

D8 Rama

D9 Saalibimu

D9 Gezere

D9 Makazi

D9 Ekroni

D9 Betiseani

D9 Gati

D9 Azeka

D10 Soko

D10 Adulamu

D10 Kehila

D10 Lakisi

D11 Yatiri

D12 Beereseba

E2 Turo

E4 Kabulu

E5 Yokineamu (Yokimeamu?)

E5 Megido

E6 Taanaki

E6 Aruboti

E7 Piratoni

E8 Lebona

E8 Zereda

E8 Beteli

E9 Beti-horoni wa Kunsi

E9 Beti-horoni wa Kumtunda

E9 Geba

E9 Gibeoni

E9 Gibeya

E9 Kiriyatu-Yearimu

E9 Nobu

E9 Baalaperazimu

E9 Yerusalemu

E9 Betelehemu

E10 Tekoa

E10 Hebroni

E11 Zifi

E11 Horesi?

E11 Karimeli

E11 Maoni

E11 Esitimoa

F5 Eni-doro

F5 Sunemu

F5 Yezreeli

F6 Betesemesi

F7 Tiriza

F7 Sekemu

F8 Zaretani

F8 Silo

F8 Ofira?

F9 Yeriko

F11 Eni-gedi

G2 Abeli-beti-maaka

G2 Dani

G3 Hazoro

G3 MAAKA

G5 Lodebara (Dibri)

G5 Rogelim

G6 Abelemehola

G7 Sukoti

G7 Mahanaimu

H1 SURIYA

H4 GESURI

H6 Ramoti Gileadi

H8 Raba

H9 Medeba

H11 Aroeri

H12 MOABU

I4 Helamu?

I9 AMONI

[Misewu ikuluikulu]

C10 Via Maris

H6 Msewu Wachifumu

[Mapiri]

F5 Phiri la Giliboa

[Nyanja]

C8 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

F10 Nyanja ya Mchere (Nyanja Yakufa)

G4 Nyanja ya Galileya

[Kasupe kapena Chitsime]

E9 Eni-rogeli

[Zithunzi patsamba 16]

Kumanja: Chigwa cha Ela, kuyang’ana chakum’maŵa kumapiri a Yuda

M’munsimu: Njira zinathandiza kwambiri pa kayendedwe m’Dziko Lolonjezedwa

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena