Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 28-29
  • Yesu “m’Dziko la Ayuda”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu “m’Dziko la Ayuda”
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • ‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • B10 Dziko la Isiraeli mu Nthawi ya Yesu
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 28-29

Yesu “m’Dziko la Ayuda”

Dziko Lolonjezedwa M’Nthawi ya Yesu

POLALIKIRA kwa Korneliyo, mtumwi Petro anatchulapo zimene Yesu anachita “m’dziko la Ayuda ndi m’Yerusalemu.” (Mac. 10:39) Kodi mukuganiza kuti ndi madera ati amene Yesu anafikako pochita utumiki wake wosaiŵalika m’mbiri ya anthu?

“Dziko la Ayuda” linaphatikizapo Yudeya, kumene Yesu anagwirako ntchito ina ya Mulungu. (Luka 4:44) Yesu atabatizidwa, anatha masiku 40 ali m’chipululu cha Yuda (kapena, Yudeya), chomwe chinali dera louma kwambiri ndi lopanda anthu kumene ogalukira ndi achifwamba anali kukonda kukhala. (Luka 10:30) Panthaŵi ina, Yesu anali kupita chakumpoto kuchokera ku Yudeya pamene analalikira mkazi wa ku Samariya pafupi ndi Sukari.—Yoh. 4:3-7.

Mukapenda Mauthenga Abwino, mudzapeza kuti Yesu anagwira ntchito kwambiri m’Galileya. Ngakhale kuti ankapita kum’mwera ku Yerusalemu kukakhala nawo pa mapwando apachaka, iye anathera mbali yaikulu ya zaka ziŵiri zoyambirira za utumiki wake kumpoto kwa Dziko Lolonjezedwa. (Yoh. 7:2-10; 10:22, 23) Mwachitsanzo, ali pa Nyanja ya Galileya kapena pafupi ndi kumeneko, iye anafotokoza ziphunzitso zambiri zapadera ndi kuchita zozizwitsa zikuluzikulu. Kumbukirani kuti anatontholetsa chimphepo panyanjapo, ndipo anayenda pamadzi akewo. Yesu analalikira ali m’bwato kwa khamu la anthu amene anakhala pagombe lansangalabwi la nyanjayo. Otsatira ake oyambirira komanso apamtima anachokera kumidzi ya asodzi ndi alimi ya pafupi ndi nyanjayo.—Marko 3:7-12; 4:35-41; Luka 5:1-11; Yoh. 6:16-21; 21:1-19.

Pamene Yesu anali kuchita utumiki wake m’Galileya anali kuchokera ku Kapernao m’mphepete mwa nyanja, “kumudzi kwawo.” (Mat. 9:1) Iye anali paphiri la pafupi ndi kumeneko pamene anapereka Ulaliki wa pa Phiri wotchuka uja. Nthaŵi zina, iye anachoka m’dera la Kapernao paulendo wa pabwato kupita ku Magadani, Betsaida, ndi madera ena apafupi.

Onani kuti “kumudzi kwawo” kwa Yesu sikunali kutali kwambiri ndi Nazarete, kumene iye anakulirako; sikunalinso kutali kwambiri ndi Kana, komwe anasandutsa madzi kukhala vinyo; kapenanso ku Nayini, kumene anaukitsa mwana wamwamuna wa mkazi wamasiye; ndiponso sikunali kutali kwambiri ndi Betsaida, kumene mozizwitsa anadyetsa amuna 5,000 ndi kuchiritsa munthu wina wakhungu.

Paskha wa mu 32 C.E. atatha, Yesu anapita kumpoto ku Turo ndi Sidoni, kumadoko a Foinike. Kenako utumiki wake unam’fikitsa ku ina ya mizinda khumi ya Agiriki yotchedwa Dekapoli. Yesu anali pafupi ndi Kaisareya wa Filipi (F2) Pamene Petro anavomereza kuti Yesu ndi Mesiya, ndipo posakhalitsa Yesu anasandulika, mwinamwake pa Phiri la Herimoni. Zimenezi zitachitika, Yesu anakalalikira m’dera la Pereya, tsidya lina la Yordano.—Marko 7:24-37; 8:27–9:2; 10:1; Luka 13:22, 33.

Mlungu wake womaliza padziko lapansi, Yesu anakhala ndi ophunzira ake m’Yerusalemu, “mzinda wa Mfumu yaikulukulu,” ndi madera ozungulira. (Mat. 5:35) Mungathe kupeza malo omwe anali pafupi omwe munaŵerengapo m’Mauthenga Abwino monga ngati Emau, Betaniya, Betefage, ndi Betelehemu.—Luka 2:4; 19:29; 24:13; Onani mapu aang’ono a “Dera la Yerusalemu,” patsamba 18.

[Mapu patsamba 29]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Promised Land (Jesus’ time)

Mmene Dzikoli Linalili Masiku A Yesu

Mizinda ya Dekapoli

E5 Hippo

E6 Pella

E6 Asikopolisi

F5 Gadara

F7 Gerasa

G5 Dion

G9 Filadelfeya

H1 Damasiko

H4 Raphana

I5 Canatha

Njira Zazikulu (Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Njira ya Pakati pa Galileya ndi Yerusalemu Imene Ambiri Anali Kudutsa (Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Njira Ina ya Pakati pa Galileya ndi Yerusalemu Yodzera ku Pereya

A11 Gaza

B6 Kaisareya

B8 Yopa

B9 Luda

B12 Beereseba

C4 Ptolemayi

C8 SAMARIYA

C8 Antipatri

C8 Arimateya

C9 Emau

C10 YUDEYA

C11 Hebroni

C12 IDUMEYA

D1 Sidoni

D2 Turo

D3 PHOENICIA

D4 GALILEYA

D4 Kana

D5 Sepphoris

D5 Nazarete

D5 Nayini

D7 Samariya

D7 Sukari

D9 Efraimu

D9 Betefage

D9 Yerusalemu

D9 Betaniya

D10 Betelehemu

D10 Herodium

D10 CHIPULULU CHA YUDEYA

D12 Masada

E4 Korazini

E4 Betsaida

E4 Kapernao

E4 Magadani

E5 Tiberiya

E5 Hippo

E6 Betaniya? (tsidya la Yordano)

E6 Asikopolisi

E6 Pella

E6 Salemu

E6 Ainoni

E9 Yeriko

F1 ABILENE

F2 Kaisareya wa Filipi

F4 Gamala

F5 Abila?

F5 Gadara

F7 PEREYA

F7 Gerasa

G3 ITUREYA

G5 Dion

G6 DEKAPOLI

G9 Filadalfeya

H1 Damascus

H3 TRAKONITI

H4 Raphana

H12 ARABIYA

I5 Canatha

[Mapiri]

D7 Phiri la Ebala

D7 Phiri la Gerizimu

F2 Phiri la Herimoni

[Nyanja]

B6 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

E4 Nyanja ya Galileya

E10 Nyanja ya Mchere (Nyanja Yakufa)

[Mitsinje]

E7 Mtsinje wa Yordano

[Akasupe ndi Zitsime]

D7 Chitsime cha Yakobo

[Chithunzi patsamba 28]

Nyanja ya Galileya. Kapernao ali chakuno kumanzere. Maloŵa amaoneka chonchi mukayang’ana kum’mwera chakumadzulo kudutsa Chidikha cha Genesarete.

[Chithunzi patsamba 28]

Asamariya anali kulambira m’Phiri la Gerizimu. Chakutsogoloko kuli Phiri la Ebala

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena