Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w90 10/1 tsamba 3
  • Kodi Mumalakalaka Nthaŵi Pamene . . .

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumalakalaka Nthaŵi Pamene . . .
  • Nsanja ya Olonda​—1990
  • Nkhani Yofanana
  • Uchigaŵenga Utha Posachedwapa!
    Galamukani!—2001
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2005
  • Kodi N’chiyani Chimayambitsa Vuto la Kusowa Pokhala?
    Galamukani!—2005
  • Kodi Uchigawenga Udzatha?
    Nkhani Zina
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda​—1990
w90 10/1 tsamba 3

Kodi Mumalakalaka Nthaŵi Pamene . . .

□ mungadzimve kukhala wotetezereka ndi wachisungiko m’nyumba mwanu​—mosasamala kanthu kuti ndi nthaŵi yanji?

□ simudzafunikira maloko, mizati, mabelu ochenjeza kuti kwabwera mbala, magalasi osunzumirira alendo, malinga, alonda, agalu olonda, ndi zochinjiriza zina?

□ mungayende m’makwalala muli nokha m’chisungiko changwiro, ngakhale usiku?

□ mankhwala ogodomalitsa ndi mavuto onse ogwirizana nawo adzakhala zinthu zakale?

□ nkhondo zonse zidzaleka, ndipo zida sizidzapangidwa kapena kukundikidwa?

□ simudzafunikira kudandaula ndi chakudya, mpweya, ndi madzi oipitsidwa?

□ uchigaŵenga, kugwidwa ukapolo, ndi ziwopsyezo za mabomba zidzachotsedwa kotheratu?

□ chuma chachilengedwe cha dziko lapansi chidzachinjirizidwa, kusungidwa, ndi kugwiritsiridwa ntchito mwanzeru kaamba ka ubwino wa onse?

□ umbombo ndi dyera zidzaleka kukhala chisonkhezero cha anthu?

□ ana adzasunga kupanda liŵongo kwawo ndikukhala aulemu kwa ena ndi katundu wawo?

□ akazi sadzatsenderezedwa ndi kuvutitsidwa?

□ malamulo ndi mpambo wa zitsogozo udzakhala wabwino ndipo udzaperekedwa mwachilungamo kaamba ka ubwino wa onse?

□ boma lidzapanga zosankha zozikidwa pa zosoŵa zenizeni ndipo osati pa ndale zadziko?

□ ufulu ndi kulingana sikudzanenedwa kokha komanso kuchitidwa?

□ umphaŵi udzatheratu, koma onse adzakhala ndi zonse zofunikira kaamba ka thanzi lawo, umoyo wabwino, ndi chimwemwe?

□ ana adzafunidwa ndi kusamaliridwa ndipo sadzaipsyidwa kapena kutaidwa konse?

□ matenda ndi imfa zidzagonjetsedwa, ndipo sipadzakhalanso miliri yowopsya?

□ aliyense amene mukumana naye adzakhala wachifundo, wothandiza, ndipo wodalirika?

□ moyo wa aliyense udzakhaladi wamtengo wake, ndipo onse angapeze chimwemwe chosatha?

□ chipembedzo sichidzakhalanso mphamvu yogaŵanitsa, yotsogolera ku kudzikweza, udani, ndi nkhondo?

□ onse adzakhala ndi malo okwanira ndi osangalatsa okhalamo, ndipo kupanda pokhala kudzakhala chinthu chakale?

Ngati munganene kuti inde ku lirilonse la mafunso ali pamwambawo, mudzasangalala kuŵerenga nkhani zomwe zikutsatira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena