Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w05 11/15 tsamba 3
  • Kodi Mdyerekezi Alikodi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mdyerekezi Alikodi?
  • Nsanja ya Olonda—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Kodi Amene Akulamulira Dzikoli Ndani Kwenikweni?
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Mdani wa Moyo Wosatha
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2005
w05 11/15 tsamba 3

Kodi Mdyerekezi Alikodi?

KODI mukamaganiza za Mdyerekezi, mumati ndi ndani? Kodi mumaganiza kuti alikodi, ndipo amayesa anthu kuti achite zinthu zoipa? Kodi mumaganiza kuti Mdyerekezi amangoimira khalidwe lililonse loipa? Kodi Mdyerekezi n’ngofunika kumuopa, kapena kodi tingangofunika kumunyalanyaza ngati kuti ndi nkhambakamwa chabe kapena kuti yangokhala nthano basi? Kodi liwu lakuti “mdyerekezi” limaimira mphamvu inayake yosaoneka ya m’chilengedwe koma yowononga? Kapena kodi mawuwo, amangoimira makhalidwe oipa amene anthu ali nawo, monga mmene amanenera akatswiri amakono a zaumulungu?

N’zosadabwitsa kuti anthu amasiyana maganizo pa nkhani yakuti kodi Mdyerekezi ndi ndani kwenikweni. Tangoganizani mmene zingakhalire zovuta kudziwa zoona zenizeni zokhudza winawake amene amatchuka kuti ndi katswiri pankhani yodzibisa. Ndipo zingakhale zovuta kwambiri makamaka ngati munthuyo amayesetsa kudzibisa ngati kuti wavala chinyawu. Baibulo limafotokoza kuti Mdyerekezi ali wotero. Ponena za iyeyu monga Satana, Baibulo limati: ‘Satana adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.’ (2 Akorinto 11:14) Choncho ngakhale kuti ndi woipa, Mdyerekezi amadzionetsa ngati wabwino n’cholinga chakuti akope anthu ena. Ndipo akangowapangitsa kukhulupirira kuti iyeyo kulibe, m’pamene zimagwirizana bwino kwambiri ndi zofuna zake.

Ndiyeno kodi Mdyerekezi, ndi ndani kwenikweni? Kodi anakhalapo liti, ndipo zinatani kuti akhalepo? Kodi ndi motani mmene amasokeretsera anthu masiku ano? Kodi pali chilichonse chimene tingachite ngati chilipo, kuti asatisokeretse? Baibulo lili ndi mbiri yolondola bwino ya Mdyerekezi kuchokera pamene anayambira, ndiponso limapereka mayankho olondola a mafunso omwe ali pamwambawa.

[Chithunzi patsamba 3]

N’zovuta kwambiri kuzindikira munthu amene sakufuna m’pang’onong’ono pomwe kuti ena amuzindikire makamaka ngati wavala chinyawu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena