Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w14 4/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2014
w14 4/1 tsamba 16
Dzanja la Yesu akupukuta dziko

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Yesu adzachita chiyani m’tsogolomu?

M’chaka cha 33 C.E., Yesu anaphedwa, kuukitsidwa kenako n’kukwera kumwamba. Patapita nthawi Yesu anapatsidwa mphamvu zolamulira monga Mfumu. (Danieli 7:13, 14) M’tsogolomu, Yesu monga Mfumu adzabweretsa mtendere padzikoli komanso adzathetsa umphawi.—Werengani Salimo 72:7, 8, 13.

Monga Mfumu, Yesu adzayeretsa dziko lopanda chilungamoli

Yesu monga wolamulira, adzachitira anthu zinthu zodabwitsa padzikoli. Adzagwiritsa ntchito mphamvu zimene Atate wake anamupatsa ndipo adzathandiza anthu kukhala angwiro. Anthu adzasangalala kwambiri padziko lapansili chifukwa sadzakalamba komanso kufa.—Werengani Yohane 5:26-29; 1 Akorinto 15:25, 26.

Kodi Yesu akuchita chiyani panopa?

Panopa Yesu akutsogolera ntchito yolalikira imene otsatira ake oona akugwira padziko lonse. Otsatira akewa amafikira anthu n’cholinga chowauza zimene Baibulo limanena zokhudza Ufumu wa Mulungu. Yesu ananena kuti adzapitirizabe kutsogolera ntchito imeneyi mpaka pamene Ufumu wa Mulungu udzawononge maboma a anthu.—Werengani Mateyu 24:14; 28:19, 20.

Yesu akuthandizanso anthu kuti akhale ndi moyo wabwino pogwiritsa ntchito mpingo woona wachikhristu. Iye adzapitirizabe kutsogolera Akhristu amenewa mpaka pa nthawi imene azidzawononga dziko loipali, n’kuwalowetsa m’dziko latsopano.—Werengani 2 Petulo 3:7, 13; Chivumbulutso 7:17.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 8 wa buku lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova.

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena