Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 7/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Kodi Chabwino Chidzagonjetsadi Choipa?
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 7/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

N’chiyani chimachititsa kuti anthu azichita zoipa?

Yesu akukana pamene Mdyerekezi akumuuza kuti amupatsa maufumu onse a padziko lapansi

Kodi ndi ndani amene anayesa Yesu kuti achite zoipa?—Mateyu 4:8-10

Anthufe timafuna titamachita zinthu mwamtendere, moona mtima komanso mwachifundo. Nanga n’chifukwa chiyani padzikoli pamachitika zinthu zopanda chilungamo, zachiwawa komanso anthu amachitirana nkhanza? Nthawi zambiri timamva zokhudza zinthu zoopsa monga nkhondo kapenanso kuzionera pa TV. Kodi pali winawake amene amapangitsa kuti anthu azichita zoipa?—Werengani 1 Yohane 5:19.

Kodi Mulungu anatilenga anthufe ndi maganizo ofuna kuchita zoipa? Ayi, chifukwa Baibulo limati Yehova Mulungu analenga anthu m’chifaniziro chake. Izi zimapangitsa kuti tizitha kusonyeza chikondi ngati mmene iye amachitira. (Genesis 1:27; Yobu 34:10) Komatu Mulungu anatipatsa ufulu wosankha ndipo zimenezi zimasonyeza kuti amatilemekeza. Makolo athu oyambirira anasankha molakwika chifukwa sanamvere Mulungu. Zimenezi zinapangitsa kuti asamakwanitsenso kutsanzira makhalidwe abwino a Mulungu popanda kulakwitsa chilichonse. N’chifukwa chake anthufe timachita zoipa.—Werengani Deuteronomo 32:4, 5.

Kodi anthu adzasiya kuchita zoipa?

Mulungu amafuna kuti tizichita zinthu zabwino osati zoipa. (Miyambo 27:11) Choncho amatiphunzitsa zimene tingachite kuti tizipewa kuchita zoipa komanso kuti tikhale osangalala. Koma panopa, sitingathe kutsanzira bwinobwino chikondi cha Mulungu.—Werengani Salimo 32:8.

Ngakhale kuti zinthu zoipa zachuluka masiku ano, Mulungu wazilola kwa kanthawi ndithu kuti aliyense aone zotsatira za kuchita zinthu zoipa. (2 Petulo 3:7-9) Posachedwapa, padziko lonse padzakhala anthu osangalala komanso omvera Mulungu.—Werengani Salimo 37:9-11.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 3 m’buku lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena