Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp16 No. 4 tsamba 3
  • Kodi Kudziwa Mmene Baibulo Linapulumukira N’kothandiza?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Kudziwa Mmene Baibulo Linapulumukira N’kothandiza?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Baibulo Lakumana ndi Zambiri
    Galamukani!—2007
  • Kumenyera Nkhondo Kukhala ndi Moyo kwa Baibulo
    Baibulo—Kodi Ndilo Mawu a Mulungu Kapena a Munthu?
  • A3 Zimene Zinachitika Kuti Baibulo Lisungike Mpaka Pano
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Mulungu Akutiuza za Zifuno Zake
    Kodi Mulungu Amatisamaliradi?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
wp16 No. 4 tsamba 3

NKHANI YA PACHIKUTO | BAIBULO​—BUKU LOMWE LINAPULUMUKA M’ZAMBIRI

Kodi Kudziwa Mmene Baibulo Linapulumukira N’kothandiza?

Munthu wanyamula Baibulo ndipo akuoneka kuti akukayikira

Palibe buku lina lililonse la chipembedzo lomwe lingapose Baibulo, chifukwa lakhala likuthandiza anthu kuti azikhulupirira zinthu zolondola. Komanso ndi buku lokhalo limene anthu alifufuza kwambiri ndiponso kulipezera zifukwa.

Akatswiri ena amakaikira ngati uthenga wa m’Mabaibulo a masiku ano ulidi wofanana ndi womwe unali m’mipukutu yoyambirira. Mwachitsanzo, pulofesa wina wamaphunziro azachipembedzo ananena kuti: “Sitinganene motsimikiza kuti tinakoperadi uthenga wa m’Baibulo molondola chifukwa Mabaibulo ambiri ali ndi zinthu zolakwika zokhazokha. Komanso analembedwa patadutsa zaka zambiri kuchokera pamene mipukutu yoyambirira inalembedwa, choncho uthenga wake ndi wosiyana kwambiri ndi womwe unali m’mipukutuyi.”

Anthu enanso amakhulupirira kuti uthenga wa m’Baibulo unasinthidwa chifukwa ndi zomwe anaphunzitsidwa kuzipembedzo zawo. Mwachitsanzo Faizal, anauzidwa ndi anthu a m’banja lake omwe si Akhristu, kuti Baibulo ndi buku lopatulika koma linasinthidwa. Iye anati: “Chifukwa cha zimenezi, anthu akamandifotokozera zokhudza Baibulo ndinkakayikira kwambiri uthenga wake. Ndinkaona kuti si lolondola chifukwa linasinthidwa.”

Kodi kudziwa ngati Baibulo linasinthidwa kapena ayi kuli ndi phindu lililonse? Kuti mupeze yankho la funsoli, taganizirani mafunso awa: Kodi zikanakhala kuti zinthu zabwino zimene Baibulo limalonjeza sizinalembedwe m’mipukutu yoyambirira, mukanazikhulupirira? (Aroma 15:4) Zikanakhala kuti mfundo zonse za m’Mabaibulo a masiku ano ndi zolakwika, kodi mukanazigwiritsa ntchito posankha zochita pa nkhani zokhudza ntchito, banja kapena kupembedza Mulungu?

Ngakhale kuti mipukutu yoyambirira ya Baibulo sikupezeka, pali zolemba zina zakale komanso mipukutu ina yambiri ya Baibulo imene imatithandiza. Kodi zinatheka bwanji kuti mipukutuyi izipezekabe masiku ano? Funsoli ndi lofunika chifukwa anthu ena ankafuna kuithetseratu, kusintha uthenga wake komanso ikanatha kuwola. Kodi kupezeka kwa mipukutuyi kungakuthandizeni bwanji kukhulupirira kuti uthenga wa m’Baibulo ndi wolondola? Kuti mudziwe mayankho a mafunsowa, werengani nkhani zokhudza mmene Baibulo linapulumukira ku zinthu zonsezi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena