Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w17 January tsamba 32
  • Kodi Mukudziwa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mukudziwa?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Moto!—Kodi Muyenera Kuuzimitsa ndi Chida Chiti?
    Galamukani!—2001
  • Umboni Waukulu Wakuti Mulungu Amatikonda
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Abulahamu Anasonyeza Kuti Anali Wokhulupirika
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Mulungu Ayesa Abrahamu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
w17 January tsamba 32
Isaki watenga nkhuni ndipo Abulahamu watenga kamphika kokhala ndi makala

Kodi Mukudziwa?

Kodi kale anthu ankanyamula bwanji moto pa ulendo?

Lemba la Genesis 22:6 limanena kuti pamene Abulahamu ankapita kukapereka nsembe kuphiri ‘anatenga nkhuni zokawotchera nsembe n’kumusenzetsa Isaki. Iye ananyamula moto ndi mpeni wophera nyama, ndipo iwo anapitira limodzi.’

Baibulo silifotokoza mmene anthu ankayatsira moto kale. Pa nkhani ya Abulahamuyi, munthu wina ananena kuti n’zokayikitsa kuti munthu ankatha kutenga moto woyaka n’kuyenda nawo ulendo wautali. Izi zikusonyeza kuti Abulahamu sanatenge moto woyaka koma anatenga chinthu chinachake chomwe anaikamo zinthu zoti akayatsire moto.

Koma anthu ena amanena kuti kale kuyatsa moto kunali kovuta kwambiri. Amati anthu ankaona kuti bola kungopala moto kusiyana n’kuyamba kuyatsa. Choncho akatswiri ambiri amakhulupirira kuti Abulahamu anatenga chinthu changati mphika chokhala ndi chingwe cha tcheni ndipo munali makala a moto. (Yes. 30:14) Munthu akatenga makala a moto mumphika ngati umenewo ankatha kuyenda nawo kwa nthawi yaitali n’kukayatsira moto akafika kumene akupita.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena