Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/95 tsamba 2
  • Chikumbutso kwa Mlembi ndi Woyang’anira Utumiki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chikumbutso kwa Mlembi ndi Woyang’anira Utumiki
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Nkhani Yofanana
  • Kusintha Maola Ofunika kwa Apainiya
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Madalitso a Utumiki wa Upainiya
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Limbikirani Muutumiki Waupainiya
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Madalitso a Utumiki Waupainiya
    Nsanja ya Olonda—1997
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
km 3/95 tsamba 2

Chikumbutso kwa Mlembi ndi Woyang’anira Utumiki

Chaka chilichonse chilengezo cha mu Utumiki Wathu Waufumu wa February chimauza mlembi ndi woyang’anira utumiki “kupenda ntchito za apainiya okhazikika onse.” Kodi chifuno chake cha kupenda kumeneku nchiyani? Ndicho kudziŵa amene angafunikire chithandizo cha kukwaniritsa chofunika cha maola chaka chisanathe.

Apainiya okhazikika afunikira kuthera maola 1,000 chaka chilichonse mu utumiki. Pofika kumapeto kwa February, apainiya ena amapeza kuti atsala kumbuyo, ndipo zimenezi zingawafooketse. Akulu kaŵirikaŵiri angakhale othandiza kwa apainiya, akumawapatsa chilimbikitso ndi malingaliro ogwira ntchito. Zimenezi zingathandize kwambiri apainiya kukhala okhoza kukwaniritsa chofunika chawo cha pachaka, apo phuluzi akhoza kuchoka pampambo.

Apainiya amayamikiradi chisamaliro chenicheni cha akulu pankhani imeneyi. Mpingo udzapindulanso mwa kukhala ndi apainiya amene ali achimwemwe mu utumiki wawo, akumamamatira mokhulupirika pa ntchito yawo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena