Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/97 tsamba 1
  • Misonkhano Imafulumiza ku Ntchito Zabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Misonkhano Imafulumiza ku Ntchito Zabwino
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Misonkhano ya Mboni za Yehova Ingakuthandizeni Bwanji?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kusonkhana?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Misonkhano Yokonzekera Utumiki Wakumunda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Pindulani Mokwanira ndi Misonkhano Yokonzekera Utumiki wa Kumunda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
km 8/97 tsamba 1

Misonkhano Imafulumiza ku Ntchito Zabwino

1 Mbali ziŵiri zofunika za kulambira kwathu ndizo kupezeka pamisonkhano yampingo ndi kutengamo mbali mu utumiki wakumunda. Ziŵirizi nzogwirizana. Imodzi imalimbikitsa inzake. Misonkhano yachikristu imafulumiza ku ntchito zabwino, ndipo yabwino kopambana zonse ndiyo ntchito yolalikira Ufumu ndi kupanga ophunzira. (Aheb. 10:24) Titati tileke kupezeka pamisonkhano, mwamsanga tingalekenso kulalikira chifukwa palibe chimene chidzatifulumiza kutero.

2 Pamisonkhano ya mlungu ndi mlungu, timalandirapo malangizo auzimu okonzedwa kuti atisonkhezere kulalikira. Nthaŵi zonse imatikumbutsa za kufulumira kwa nthaŵi, kutisonkhezera kukauza ena uthenga wa Baibulo wopatsa moyo. Imatilimbikitsa ndi kutipatsa nyonga yopirira pantchito yolalikira. (Mat. 24:13, 14) Mwa kupeza mipata yoyankha pamisonkhano, timazoloŵera kwambiri kusonyeza ena chikhulupiriro chathu. (Aheb. 10:23) Mwa kulembetsa Sukulu Yautumiki Wateokratiki, timaphunzira kukhala atumiki ogwira mtima ndi kuwongolera maluso athu ophunzitsa.—2 Tim. 4:2.

3 Mmene Misonkhano Yautumiki Imatisonkhezerera Kulalikira: Tonsefe timalimbikitsidwa kuŵerenga nkhani za mu Utumiki Wathu Waufumu pasadakhale. Ndiyeno chidziŵitsocho chimaloŵa m’maganizo athu pamene tili pa Msonkhano Wautumiki ndi kuona maulaliki akusonyezedwa pa pulatifomu. Pamene tili mu utumiki wakumunda, timaganiza za Utumiki Wathu Waufumu uja, ndi kukumbukira maulaliki amene anasonyezedwa aja, ndiyeno timapereka umboni wogwira mtima. Ofalitsa ambiri akhala akuchita zimenezo.

4 Pambuyo pa Misonkhano Yautumiki, ena amapangana ndi anzawo kuyendera limodzi muutumiki. Ofalitsa amakhala akuzikumbukirabe mfundo zakumundazo ndipo amasonkhezereka kuyesa kuzigwiritsira ntchito chifukwa misonkhano imeneyi yawalimbikitsa kutengamo mbali m’ntchito yolalikira mlungu uliwonse.

5 Palibe chimene chingaloŵe m’malo mwa misonkhano yathu yachikristu, kumene timakumana ndi olambira anzathu ndi kusonkhezerana ku ntchito zabwino. Ngati tifuna kuti utumiki wathu uziyenda bwino, tiyenera kumapezeka pamisonkhano yampingo nthaŵi zonse. Tiyenitu tisonyeze kuti tikuyamikira makonzedwe abwino a Yehova ameneŵa mwa ‘kusaleka kusonkhana kwathu pamodzi.’—Aheb. 10:25.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena