Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/99 tsamba 1
  • Kuwonjezera Umboni Pamene Mapeto Akuyandikira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuwonjezera Umboni Pamene Mapeto Akuyandikira
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Khalanibe Odzipereka
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Samalirani Changu Chanu
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Kodi Tingatani Kuti Tiziona Kuti Ntchito Yolalikira Ndi Yofunika Kwambiri?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • “Lalikira Mawu . . . Mwachangu”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 4/99 tsamba 1

Kuwonjezera Umboni Pamene Mapeto Akuyandikira

1 Nyengo yotuta ndi nthaŵi yosangalatsa kwambiri. Komanso ndi nthaŵi ya ntchito yambiri. Pali nthaŵi yake yosonkhanitsa mbewu. Antchito sayenera kuchita ulesi pantchito yawo.

2 Mophiphiritsa, Yesu anayerekezera “chimaliziro cha nthaŵi ya pansi pano” ndi nthaŵi yotuta. (Mat. 13:39) Tikukhala m’nthaŵi yamapeto a dongosolo la zinthu lilipoli, ndipo kwatsala nthaŵi yochepa yopereka umboni “padziko lonse lapansi.” (Mat. 24:14) Pamene mapeto akuyandikira pafupi kwambiri, tiyenera kuwonjezera mbali yathu mu utumiki. Chifukwa chiyani? Yesu anati: “Zotuta zichulukadi koma antchito ali oŵerengeka.”—Mat. 9:37, 38; Aroma 12:11.

3 Ichiteni Mwachangu: Pamene Yesu anayamba ntchito yake yaikulu yolalikira, anali ndi zaka zitatu ndi theka zokha kuti achite zimene anatumidwa. Analalikira mwachangu, akumati: ‘Kundiyenera Ine ndilalikire Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu chifukwa ndinatumidwa kudzatero.’—Luka 4:43.

4 Yesu anaphunzitsa ophunzira ake changu chofananacho. (Marko 13:32-37) N’chifukwa chake ‘masiku onse, m’Kachisi ndi m’nyumba, sanaleka kuphunzitsa ndi kulalikira za Kristu Yesu.’ (Mac. 5:42) Zinthu zosafunika kwenikweni sizinakhale zoyamba m’miyoyo yawo. Ngakhale kuti anali oŵerengeka, anali okhoza kulalikira uthenga wabwino kwa “cholengedwa chonse cha pansi pa thambo.”—Akol. 1:23.

5 Palinso chifukwa chachikulu chotipangitsa ife kukhala ndi changu chofananacho tsopano, popeza “chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi.” (1 Pet. 4:7) Yehova waika tsiku ndi ola lochotsa dongosolo la zinthu lilipoli. (Mat. 24:36) Ntchito yolalikira imalizidwa m’nthaŵi imene yatsalayi. N’chifukwa chake tiyenera kupitiriza kuwonjezera zoyesayesa zathu kuti tifikire anthu ambiri ndi uthenga wabwino.

6 Mwa kuwonjezera mbali yathu m’ntchito yochitira umboni pamene mapeto akuyandikira, tidzakhala osangalala kunena kwa Yehova, monga momwe ananenera Yesu kuti: ‘Tatsiriza ntchito imene munatipatsa kuchita.’—Yoh. 17:4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena