Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/99 tsamba 1
  • Konzekereranitu!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Konzekereranitu!
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Mulungu Akwaniritse Zofuna Zanu’
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Gwiritsani Ntchito Nthawi Yanu Mwanzeru
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Mangani Moyo Wanu pa Utumiki wa Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Kodi Mukulinganiza Kudzatani m’Chilimwe?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 5/99 tsamba 1

Konzekereranitu!

1 Gulu la Yehova limapereka pologalamu yanthaŵi zonse ya zochitika zateokalase zokonzedwa kuti zikwaniritse zosoŵa zathu zauzimu. Kuyamikira kumatisonkhezera kugwiritsa ntchito mokwanira zonse zimene zimakonzedwa, monga kuchezeredwa ndi woyang’anira woyendayenda, misonkhano yadera ndi misonkhano yachigawo, komanso zochitika zina zapadera zomwe zimakonzedwa pampingo. (Mat. 5:3) Komabe, ena amalephera kupindula ndi makonzedwe auzimu ameneŵa chifukwa cha zinthu zimene akonza kuti achite. Kodi tingachite chiyani kuti tipeŵe zimenezi? Tingatsimikize motani kuti zinthu zimene sizili zateokalase sizikudodometsa “zinthu zofunika kwambiri.”—Afil. 1:10, NW.

2 Kuganiza Mwanzeru n’Kofunika: Miyambo 21:5 imatilimbikitsa kuti: “Zoganizira za wakhama zichulukitsadi katundu; koma yense wansontho angopeza umphaŵi.” Kuti ‘tichulukitsedi katundu’ wauzimu, tiyenera kukonzekereratu mwakhama, tikumakumbukira zochitika zateokalase zomwe zakonzedwa. Kuti tipeze madalitso auzimu tiyenera kuika zochita zaumwini panthaŵi yomwe sizitilepheretsa kukapezekapo. Ngati tikonza mothamanga zinthu zaumwini zomwe tikufuna kuchita, popanda kuganizira zochitika zateokalase zomwe zakonzedwa, n’kodziŵikiratu kuti tidzakhala ‘amphaŵi’ mwauzimu.

3 Osaphonya! Tonse timakonzekera za m’tsogolo, kuphatikizapo masiku atchuthi, maulendo antchito, kukayendera achibale, ndi zina zotero. Musanakonze kapena musanatsimikize zomwe mukufuna kuchita, onani ndandanda ya zochitika zauzimu zomwe zili m’tsogolo. Ngati mupeza kuti woyang’anira dera akubwera kapena kuti nthaŵi imene inu simudzakhalapo kudzakhala msonkhano wadera, yesetsani kukonzanso zochita zanu kotero kuti mudzathe kupezekako. Amatiuziratu zochitika zikuluzikulu zomwe zichitike patsogolopa. Akulu a mpingo wanu angakuuzeni zimene zakonzedwa mumpingo wanu.

4 Mwa kuchita mwanzeru ndi kukonzekereratu zinthu zofunika kwambiri, ‘tidzadzala nacho chipatso cha chilungamo, . . . kuchitira Mulungu ulemerero ndi chiyamiko.’— Afil. 1: 11.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena