Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/00 tsamba 1
  • Kodi Mumalalikira Molimba Mtima?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumalalikira Molimba Mtima?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Nkhani Yofanana
  • Tsanzirani Yesu mwa Kulalikira Molimba Mtima
    Nsanja ya Olonda—2009
  • ‘Lankhulani Mawu a Mulungu Molimba Mtima’
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Pitirizani Kulankhula Mawu a Mulungu Molimbika Mtima
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Mupeze Mayankho a Mafunso Awa
    Pulogalamu ya Msonkhano Wadera ya 2018-2019—Wokhala ndi Woyang’anira Dera
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
km 12/00 tsamba 1

Kodi Mumalalikira Molimba Mtima?

1 Petro ndi Yohane anapitiriza kulalikira uthenga wa Ufumu molimba mtima ngakhale kuti anagwidwa ndiponso anaopsezedwa ndi otsutsa. (Mac. 4:17, 21, 31) Kodi kulalikira molimba mtima kumatanthauzanji kwa ife lerolino?

2 Kuchitira Umboni Molimba Mtima: Mawu ofanana ndi mawu akuti “kulimba mtima” ndi “kupanda mantha,” kutanthauza kuti “kusaopa kanthu, kulimba, ndi kupirira.” Kwa Akristu oona, kulalikira molimba mtima kumatanthauza kusaopa kulankhula ndi ena za uthenga wabwino nthaŵi zonse mpata ukapezeka. (Mac. 4:20; 1 Pet. 3:15) Kumatanthauza kuti sitichita manyanzi ndi uthenga wabwino. (Sal. 119:46; Aroma 1:16; 2 Tim. 1:8) Chotero, kulimba mtima ndi mkhalidwe wofunika kuti tikwaniritse ntchito yathu yolalikira uthenga wabwino wa Ufumu m’nthaŵi ya mapeto ino. Kumatisonkhezera kuuza anthu uthenga wabwino kulikonse kumene angapezeke.—Mac. 4:29; 1 Akor. 9:23.

3 Kulimba Mtima Kusukulu: Kodi mantha ndi manyazi zimakulepheretsani kulalikira kwa anzanu akusukulu? Nthaŵi zina zimavuta; ndipotu lingakhale vuto lalikulu. Komabe, Yehova adzakulimbikitsani ngati mupemphera kuti alimbitse mtima wanu kuti muthe kulalikira ena. (Sal. 138:3) Kulimba mtima kudzakuthandizani kudzidziŵikitsa kuti ndinu wa Mboni za Yehova ndiponso kupirira ponyozedwa. Ngati mulalikira kusukulu mudzapulumutsa amene amakumvetserani.—1 Tim. 4:16.

4 Kulimba Mtima Kuntchito: Kodi kuntchito mumadziŵika kuti ndinu wa Mboni za Yehova? Njira yokha imene anzanu akuntchito angamvere uthenga wabwino ingakhale kuwalalikira inuyo. Kulimba kwanu mtima kudzakuthandizaninso kupempha nthaŵi kuntchito yopita ku misonkhano yanu ya mpingo ndi misonkhano ikuluikulu.

5 Kulimba Mtima Poyesedwa: N’kofunika kukhala wolimba mtima pachitsutso. (1 Ates. 2:1, 2) Kumatithandiza kugwiritsitsa chikhulupiriro chathu pamene tikuopsezedwa, kunyozedwa, kapena pamene tikuzunzidwa kumene. (Afil. 1:27, 28) Kumatilimbitsa kuima nji pokakamizidwa kuswa miyezo ya Mulungu wathu, Yehova. Kumatilimbikitsa kusungabe mtendere pamene ena ayambitsa mikangano.—Aroma 12:18.

6 Kaya aliyense wa ife amakumana ndi mavuto amtundu wanji, tipitirizetu kulalikira uthenga wabwino molimba mtima.—Aef. 6:18-20.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena