Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/01 tsamba 1
  • Konzekerani Kuphunzira Ulosi wa Yesaya!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Konzekerani Kuphunzira Ulosi wa Yesaya!
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Tidzaphunzira Buku la Chimwemwe cha Banja
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Kuphunzira Ulosi wa Danieli!
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Phunziro Limapindulitsa
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Mmene Yehova Amatithandizira Kuti Tizipirira Mosangalala
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 7/01 tsamba 1

Konzekerani Kuphunzira Ulosi wa Yesaya!

1 “Olambira okhulupirika angakhale ndi chidaliro kuti Yehova . . . sadzalola kuti dziko la Satana likhalepobe kwa tsiku lina limodzi kupitirira pamene chilungamo chimafuna.” Ameneŵa ndi mawu olimbikitsa kwambiri. Kodi mawuŵa atengedwa kuti? Mu buku la Ulosi wa Yesaya—Muuni wa Anthu Onse 1. Kodi ulosi wa Yesaya ukutipatsa zifukwa zokhulupirira mawu olimbikitsawa? Inde, m’buku la m’Baibulo limeneli, nkhani ya chipulumutso yagogomezeredwa mwamphamvu ndiponso momveka. (Yes. 25:9) N’chifukwa chake tidzalimbikitsidwa kwambiri kuphunzira mbali imeneyi ya Mawu a Mulungu pa Phunziro la Buku la Mpingo. Kodi tidzapindula nawo mwa kupezekapo mlungu uliwonse? Kodi n’chifukwa chiyani tiyenera kuchita zimenezo?

2 Pa Yesaya 30:20, NW, Yehova amatchedwa ‘Mlangizi wathu Wamkulu.’ Mkristu aliyense ayenera kumvetsera kwambiri pamene Yehova akutilankhula kudzera m’Mawu ake ndiponso m’mabuku onena za m’Baibulo omwe “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru” amatipatsa. (Mat. 24:45; Yes. 48:17, 18) Ndi mmene lilili buku la Ulosi wa Yesaya 1. Kodi pophunzira bukuli mungapindule motani zochuluka?

3 Konzekerani Kuyankha: Mlungu uliwonse patulani nthaŵi yokwanira yokonzekera phunziro la buku. Ŵerengani ndime zonse zimene mukaphunzire. Lingalirani mofatsa mafunso operekedwawo. M’buku lanu ikani chizindikiro pamene pali mayankho. Mavesi amene agwira mawu a Yesaya alembedwa m’zilembo zakuda kwambiri. Aŵerengeni mofatsa. Malemba ena onse amene angoikidwapo, aŵerengeni kuti muone kugwirizana kwake ndi nkhani imene mukuphunzira. Sinkhasinkhani zimene mukuphunzira. Ndiyeno ku phunziro lanu la buku katulutseni zimene munapeza pokonzekera.

4 Mbale amene amachititsa phunziro la buku athandize opezeka paphunzirolo kugwiritsa ntchito Baibulo ndiponso kuzindikira kufunika kwa zimene akuphunzirazo. Ngati ndinu woyamba kuyankha funso pandime, yankhani mwachidule ndiponso mosapita m’mbali. Ngati wina wachita kale zimenezi, mungawonjezere pamfundo imene mukukambirana. Mukhoza kufotokoza kugwirizana kwa lemba lofunika kwambiri pandimeyo ndi mutu umene mukuphunzira. Yesetsani kuyankha m’mawu anuanu, ndipo sangalalani mwa kutenga mbali m’makambiranowo.

5 Tonse pamodzi tipende mwachidwi uthenga wapadera mu buku la Yesaya. Udzatilimbikitsa kuti tikhale osangalala tsiku lililonse poyembekeza chipulumutso cha Yehova.—Yes. 30:18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena