Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/01 tsamba 8
  • Kodi Cholinga Chathu N’chiyani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Cholinga Chathu N’chiyani?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kutsogoza Ophunzira ku Gulu la Dzina lathu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Thandizani Ena Kupezeka Pamisonkhano
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Mmene Tingapangire ophunzira ndi Buku la Chidziŵitso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
  • Muzithandiza Ophunzira Baibulo Anu Kuti Afike Pobatizidwa​—Gawo 1
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 10/01 tsamba 8

Kodi Cholinga Chathu N’chiyani?

1 N’chifukwa chiyani timachititsa maphunziro a Baibulo? Kodi timangofuna kuti anthu adziŵe Baibulo, titukule miyoyo ya anthu, kapena kuti adziŵe bwino zinthu za m’tsogolo? Ayi, si zimenezo. Cholinga chathu chenicheni ndicho kupanga ophunzira a Yesu Kristu. (Mat. 28:19; Mac. 14:21) N’chifukwa chake anthu amene timaphunzira nawo afunika kusonkhana ndi mpingo. Kukula kwawo mwauzimu kumayenderana ndi mmene akulidziŵira bwino gulu lachikristu.

2 Mmene Tingachitire Zimenezi: Mukangoyamba kuphunzira naye, musaleke kulimbikitsa wophunzirayo kupezeka pa misonkhano yampingo. (Aheb. 10:24, 25) M’fotokozereni mmene zimenezi zingalimbitsire chikhulupiriro chake, kumuthandiza kuchita zofuna za Mulungu, ndi kumuthandiza kupeza mabwenzi abwino amene akufunanso kutamanda Yehova. (Sal. 27:13; 32:8; 35:18) Kukonda ndi kuyamikira kwanu mpingo ndi misonkhano kudzam’limbikitsa kuti azipezekapo.

3 Anthu atsopano afunika kumvetsetsa kuti gulu la Yehova ndi la abale apadziko lonse. Ngati n’kotheka, aonetseni vidiyo ya Jehovah’s Witnesses—The Organization Behind the Name ndi Our Whole Association of Brothers. Athandizeni kuzindikira kuti Yehova akugwiritsa ntchito anthu odzipatulira miyandamiyanda padziko lonse kukwaniritsa zofuna zake. Auzeni atsopanowo kuti akuitanidwa kuti nawonso atumikire Mulungu.—Yes. 2:2, 3.

4 Zimasangalatsa kwambiri kuona wophunzira Baibulo akukhala wophunzira weniweni wa Yesu. Chimenechi ndiye cholinga chathu.—3 Yoh. 4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena