Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 10/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct.15

“Kodi mungawafotokozere bwanji ana kapena anthu ena chifukwa chake masiku ano pamachitika zinthu zambiri zoipa? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limayankha funso lakuti, ‘Kodi Ndani Amene Amachititsa Kuipa Konseku?’ [Ŵerengani 1 Yohane 5:19.] Magazini ya Nsanja ya Olonda iyi ikuthandizani kudziŵa woipa ameneyu ndiponso momwe tingam’kanire.”

Galamukani! Oct. 8

“Anthu ambiri masiku ano akuda nkhaŵa kwambiri ndi zigaŵenga, komanso zida zofalitsa tizilombo topereka matenda. Kodi mukuganiza kuti maboma a anthu angathetse uchigaŵenga padziko lapansi pano? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limanena zimene Mulungu akufuna kuchita. [Ŵerengani Ezekieli 34:28.] Galamukani! iyi ikufotokoza mfundo zina zokhudza nkhaniyi.”

Nsanja ya Olonda Nov. 1

“Ambirife timayesetsa kukhala bwino ndi anthu ena. Koma simungakane kuti zimenezi n’zovuta nthaŵi zambiri, si choncho? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limafotokoza chifukwa chake zinthu zili chonchi. [Ŵerengani Yakobo 3:2.] Nkhani iyi ikusonyeza mmene kupepesa kungathandizire kukhazikitsa ndi kusungitsa mtendere.”

Galamukani! Oct. 8

“Masiku ano zikuoneka kuti mabanja a kholo limodzi lokha akuchuluka kwambiri. Baibulo limasonyeza kuti Mlengi wathu amawamvera chisoni mabanja otereŵa. [Ŵerengani Salmo 146:9.] Galamukani! iyi ikusonyeza momwe mfundo za makhalidwe abwino za m’Baibulo zingathandizire makolo ameneŵa kulera ana awo bwinobwino.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena