Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/06 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
km 10/06 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct.15

“Popeza Mulungu ali kumwamba, ena amaganiza kuti n’zosatheka kum’dziwa bwino. Kodi munayamba mwaganizapo choncho? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Yohane 17:3.] Magazini ino ikulongosola mmene tingam’dziwire bwino Mulungu.”

Galamukani! Oct.

“Ambirife taferedwapo anthu amene tinali kuwakonda. Kodi mukuganiza kuti pali zinthu zomwe tingachite kuti tithandize anthu akufawa? [Yembekezani ayankhe.] Magazini ino ili ndi yankho la m’Baibulo la funso limenelo. Ikulongosolanso lonjezo lotonthoza ili.” Werengani Yohane 5:28, 29. Ndiyeno pitani pa nkhani yomwe ikuyambira pa tsamba 10.

Nsanja ya Olonda Nov. 1

“Masiku ano, pali maganizo osiyanasiyana pankhani yolera ana. Kodi mukuganiza kuti n’zotheka kuti makolo apeze malangizo odalirika pa nkhani imeneyi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Salmo 32:8.] Magazini iyi ili ndi malangizo abwino a m’Baibulo pa nkhani yolera ana.”

Galamukani! Nov.

“Kodi munayamba mwadzifunsapo kuti ngati Mulungu wachikondi, wachilungamo ndi wamphamvu alipodi, n’chifukwa chiyani pali mavuto ochuluka chonchi? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zomwe lemba ili limanena za yemwe amayambitsa kuvutika. [Werengani 1 Yohane 5:19.] Magazini ino ikulongosola mfundo za m’Baibulo zosonyeza zomwe Mulungu akuchita kuti athetse mavuto.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena