Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 10/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct. 15

“Zinthu zambiri zimene timasankha zimakhudza moyo wathu kwa nthaŵi yaitali. Kodi n’chiyani chingatithandize kupeŵa kusankha molakwika? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 3:6.] Magazini ya Nsanja ya Olonda iyi ili ndi mfundo zisanu zochokera m’Baibulo zimene zingatithandize kusankha mwanzeru.”

Galamukani! Oct. 8

“Timachita chidwi kwambiri tikaona mmene zinyama zimalankhulirana. Koma kodi mukudziŵa kuti m’njira zina anthu ndi apadera? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Salmo 65:2.] Mosiyana ndi zinyama, timalakalaka kulankhula ndi Mulungu. Magazini iyi ikufotokoza mmene tingamalankhulirane bwino ndi anthu komanso ndi Mulungu.”

Nsanja ya Olonda Nov. 1

“Tonsefe nthaŵi inayake munthu amene tinkamukhulupirira anatikhumudwitsapo. Kodi munayamba mwadzifunsapo kuti, ‘Kodi pali winawake amene ndingamukhulupirire?’ [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 3:5.] Magazini iyi ikufotokoza chifukwa chake tingakhulupirire Mulungu ndi mtima wathu wonse. Ikufotokozanso mmene tingadziŵire anthu amene tingawakhulupiriredi.”

Galamukani! Oct. 8

“Kodi mwamva zoti alimi ambiri zikuwavuta kuti azidalira ulimi pa moyo wawo? [Yembekezani ayankhe.] Magazini ya Galamukani! iyi ikufotokoza za vuto limeneli komanso za lonjezo limene lili m’Baibulo loti zinthu zisintha m’tsogolo muno. [Ŵerengani Salmo 72:16.] Ndikadzabweranso, ndikufuna ndidzakufotokozereni mmene Mulungu adzachitire zimenezi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena